Ndandanda ya Mlungu wa January 6
MLUNGU WOYAMBIRA JANUARY 6, 2014
Nyimbo Na. 120 ndi Pemphero
□ Phunziro la Baibulo la Mpingo:
jr mutu 6 ndime 1-6 (Mph. 30)
□ Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Genesis 1-5 (Mph. 10)
Na. 1: Genesis 4:1-16 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: Anthu Amene Ali M’chipembedzo Choona Amalalikira za Ufumu wa Mulungu Mwakhama—rs tsa. 90 ndime 4 (Mph. 5)
Na. 3: Kodi Mkhristu Ayenera Kuchita Chiyani Akasemphana Maganizo Ndi Mkhristu Mnzake pa Nkhani za Bizinezi?—lv tsa. 222-223 (Mph. 5)
□ Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 5: Zimene Munganene Pogawira Magazini mu January. Nkhani yokambirana. Kwa masekondi 30 mpaka 60, fotokozani chifukwa chake magaziniwo angakhale othandiza m’gawo lanu. Kenako, pogwiritsa ntchito nkhani zoyambirira za mu Nsanja ya Olonda, pemphani omvera kuti anene funso lochititsa chidwi ndiponso lemba limene angawerenge pogawira magaziniwo. Chitaninso chimodzimodzi ndi nkhani zoyambirira m’magazini ya Galamukani! Ngati nthawi ilipo mungachitenso zimenezi ndi nkhani ina imodzi m’magazini ya Nsanja ya Olonda kapena Galamukani! Chitani chitsanzo chosonyeza mmene mungagawirire magazini iliyonse.
Mph. 10: Zosowa za pampingo.
Mph. 10: Kodi Tikuphunzirapo Chiyani? Nkhani yokambirana. Werengani 1 Akorinto 9:19-23. Kambiranani mmene lemba limeneli lingatithandizire mu utumiki wakumunda.
Nyimbo Na. 7 ndi Pemphero