Ndandanda ya Mlungu wa February 3
MLUNGU WOYAMBIRA FEBRUARY 3
Nyimbo Na. 76 ndi Pemphero
Phunziro la Baibulo la Mpingo:
jr mutu 7 ndime 1-6 (Mph. 30)
Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Genesis 21-24 (Mph. 10)
Na. 1: Genesis 23:1-20 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: Chifukwa Chimene Yesu Ankavalira Matupi Anyama—rs tsa. 108 ndime 3–tsa. 109 ndime 2 (Mph. 5)
Na. 3: Khalani Ndi Chikhulupiriro Chimene Chimakondweretsa Mulungu—bh tsa. 176 ndime 5-7 (Mph. 5)
Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 10: Zimene Munganene Pogawira Magazini a February. Nkhani yokambirana. Yambani ndi kuchita chitsanzo cha mmene tingagawirire magaziniwo pogwiritsa ntchito zitsanzo za ulaliki zimene zili patsamba lino. Kenako werengani zitsanzo za ulalikizo. Muziwerenga chiganizo chimodzi kapena ziwiri n’kupempha omvera kuti afotokozepo. Chitani zimenezi mpaka mutamaliza kuwerenga mawu onse. Kumbutsani ofalitsa onse kuti azinena zimenezi m’mawu awoawo, akhoza kusintha chitsanzochi mwina ndi mwina kuti chigwirizane ndi mwininyumba kapenanso akhoza kukonza chitsanzo chawo. Pomaliza, limbikitsani ofalitsa onse kuti ayenera kuwerenga magaziniwo n’cholinga choti awadziwe bwino komanso alimbikitseni kuti adzagawire nawo magaziniwa.
Mph. 10: Zosowa za pampingo
Mph. 10: Mudzawazindikira Ndi Zipatso Zawo. (Mat. 7:16) Nkhani yokambirana yochokera mu Buku Lapachaka la 2013, tsamba 47 ndime 1-2 komanso tsamba 52 ndime 1-6. Pemphani omvera kuti anene zimene tikuphunzirapo.
Nyimbo Na. 25 ndi Pemphero