Ndandanda ya Mlungu wa March 23
MLUNGU WOYAMBIRA MARCH 23
□ Phunziro la Baibulo la Mpingo:
cl-CN mutu 16, ndime 12-22, ndi bokosi
□ Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Genesis 47-50
Na. 1: Genesis 48:1-16
Na. 2: Kodi Mdyerekezi Tizimuopa?
Na. 3: Angelo a Mulungu Amatithandiza (lr-CN mutu 11)
□ Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 5: Zilengezo.
Mph. 10: Konzekerani Kugawira Nsanja ya Olonda ya April 1 ndi Galamukani! ya April. Kukambirana ndi omvera. Pambuyo pofotokoza mwachidule zimene zili m’magaziniwo, pemphani omvera kuti atchule nkhani zimene akufuna kudzagwiritsira ntchito m’gawo lanu ndiponso chifukwa chake. Kodi angagwiritsire ntchito mafunso ndi malemba otani posonyeza nkhanizo? Chitani zitsanzo zosonyeza mmene tingagawirire magazini iliyonse. Mu chitsanzo chimodzi, musonyeze mmene tingayambitsire phunziro pa ulendo wobwereza.
Mph. 10: Zosowa za pampingo.
Mph. 10: Sonyezani Ulemu mwa Kumvetsera Mosamala ndi Kuganizira Malingaliro a Mwininyumba. Nkhani ndi kukambirana ndi omvera, yochokera m’buku la Sukulu ya Utumiki, masamba 186-187. Chitani chitsanzo chosonyeza mmene tingagwiritsire ntchito malangizo amenewa. Kenako, pemphani omvera kuti afotokoze chifukwa chake akuganiza kuti zimene wofalitsa wachita m’chitsanzochi ndi zothandiza kwambiri.