‘Pitirizani Kukhala Wowongolereka’
“KODI ndinu wotsimikiza kuti sitidzawaphonya?” Wokweramo anafunsa ofisala wamkulu wa chombo. Pamene chombo chaching’onocho chinakhota ndikuloŵa Pamafunde amphamvu a nyanja ya South Atlantic, kunawonekera kukhala pafupifupi chozizwitsa kwa mkazi wokweramoyo kuti akafika pa kadontho kali pa mapu kamene kanali malo amene ankapitapo.
Chotero ofisala wamkuluyo anaitanira mkaziyo pa malo oyendetsera namfotokozera mmene ziwiya zoyendera pamadzi zimagwirira ntchito—gyro compasses, radar, zolandilira zizindikiro za satellite, ndipo ngakhale sextant yozoloŵereka. Ngakhale kuti kufotokoza kwa ziwiyazo sikunali komvetsetseka kwenikweni kwa iye, anamvetsetsa lamulo lalikulu loyendera pamadzi: kuwongolera kayendedwe. Mothandizidwa ndi giyala yake yowongolerera, kaputeniyo anatha kupewa kukankha kwamphamvu kwa madzi oyenda anyanja ndi kwa chimphepo mwakumawongolera mosalekeza. Popanda kuwongolera koteroko, iwo akanaphonya malo amene ankapitako, ndimakilomita ambirimbiri.
Akristu ali ngati zombo zoyenda m’nyanja ya anthu. Chonulirapo chathu ndicho ‘kupezedwa ndi [Yehova] mumtendere, opanda banga ndi opanda chilema.’ (2 Petro 3:14) Koma mofanana ndi chombo, pamakhala mphamvu zolimbana nazo—mkati ndi kunja—zimene zimayesa kutichotsa panjira. Pamenepa, ngoyenerera chotani nanga mawu a mtumwi Paulo kwa Akorinto akuti: “Ichinso tipempherera, kukhala owongolereka. . . . Pitirizani kukhala . . . owongolereka.”—2 Akorinto 13:9, 11, NW.
Zimene Kuwongolereka Kumaphatikizapo
Liwu Lachigiriki lotembenuzidwa panopa kukhala “kuwongolera” limasonya ku kuika chinthu “m’njira yoyenera.” (Onani mawu amtsinde a Reference Bible.) M’malemba ena a Baibulo, lagwiritsiridwa ntchito kufotokoza kubwezeretsa chinthu kumkhalidwe wake woyenera. Mwachitsanzo, pa Mateyu 4:21, liwu lofananalo lagwiritsiridwa ntchito kufotokoza “kusoka” makoka. (Kingdom Interlinear) Pamenepa, kodi kukhala wowongolereka kumatanthauzanji kwa Akristu?
Eya, lingalirani Akristu a ku Korinto amene Paulo ankalembera. M’kalata yoyambirira kwa iwo, Paulo anatchula mikhalidwe ingapo yosayenera imene inali mumpingomo: mipatuko, kulekerera chisembwere chakugonana, milandu pakati pa abale, kusasonyeza ulemu ku Chakudya Chamadzulo cha Ambuye, ndipo ngakhale misonkhano yosalongosoka. (1 Akorinto 1:10-13; 5:1; 6:1; 11:20, 21; 14:26-33) Chotero Akristu anafunikira “kukonza” mkhalidwe kumeneko, ndiko kuti, kuika “m’njira yoyenera” malamulo amakhalidwe abwino aumulungu.
Kalata yachiŵiri ya Paulo kwa iwo imasonyeza kuti iwo anachita ndendende zimenezo. (2 Akorinto 7:11) Komabe, Paulo anadziŵa kuti zipsinjo zochokera ku dziko, zochokera kwa Satana, ndi zochokera ku zikhoterero zamatupi awo zikapitirizabe kumawapambutsa pa njira nthaŵi ndi nthaŵi. Motero, iye anapatsa uphungu woyenerera wa ‘kupitirizabe kukhala owongolereka.’
Kufunika kwa Kuwongolereka Lerolino
Mofananamo mboni za Yehova lerolino ziyenera kupitirizabe kukhala zowongolereka. Satana Mdyerekezi ‘akuchita nkhondo’ nafe, akugwira ntchito mwamphamvu kufuna kuswa umphumphu wathu. (Chibvumbulutso 12:17; Aefeso 6:12) Tazingidwanso ndi dongosolo lazinthu la dziko lonse limene limachita zinthu “monga mwa mkulu wa ulamuliro wa mlengalenga.” Anzathu apantchito ndi apasukulu angakhale anthu ‘amayendedwe ogwirizana ndi zikhumbo za thupi lawo, omachita zinthu zofunidwa ndi matupi awo.’ (Aefeso 2:2, 3) Tirinso ndi nkhondo yosalekeza yolimbana ndi zikhoterero zauchimo zachibadwa. (Aroma 7:18-25) Popanda kuwongoleredwa kwanthaŵi ndi nthaŵi, tingapambutsidwe panjira mosavuta.
Chokumana nacho cha mtumwi Petro chimafotokoza mwafanizo bwino lomwe ponena za chimenechi. Atadziŵikitsa Yesu molondola monga “Kristu, Mwana wa Mulungu wamoyo,” Petro anayamikiridwa ndi mawu akuti: ‘Ndiwe wodala, Simoni Bar-Yona: pakuti thupi ndi mwazi sizinakuululira ichi, koma Atate wanga wa kumwamba.’ (Mateyu 16:16, 17) Mwachiwonekere, kulingalira kwa Petro kunali m’njira yoyenera. Komabe, mkati mwa nthaŵi yokutidwa ndi mavesi asanu ndi limodzi otsatira, iye anafunikira kudzudzulidwa mwamphamvu ndi Yesu! Atamva kuti Kristu ‘akazunzidwa kwambiri . . . ndi kukaphedwa,’ Petro analangiza Yesu kuti: ‘Dzichitireni chifundo, Ambuye; sichidzatero kwa inu ayi.’ Yesu momdula mawu anayankha nati: ‘Pita kumbuyo kwanga, Satana iwe; ndiwe chondikhumudwitsa ine, chifukwa sumasamalira za Mulungu, koma za anthu.’—Mateyu 16:21-23.
Petro ankaganizira mwalingaliro lakuthupi. Malingaliro ake ndi maganizo zinafunikira kuwongoleredwa. Kodi sizirinso choncho kwa tonsefe nthaŵi ndi nthaŵi? Kodi sitiri okhoterera kumawona zinthu mwalingaliro lathulathu mmalo mwa la Mulungu? Chotero, nthaŵi ndi nthaŵi tifunikira kuwongoleredwa. Mofanana ndi chombo panyanja, kuwongolera koteroko panthaŵi zina kungakhale kwakung’ono kwambiri, pafupifupi kosawonekera. Koma kungatanthauze kufika kumene tikupitako kapena kusweka kwa chombo kwauzimu. Ndithudi, kuwongolera kwakung’ono tsopano kungachinjirize kupanga kuwongokera kwakukulu—mwinamwake kopweteka—kwamtsogolo.
Miyezo ya Mulungu
Ngati ziwiya zoyendera pamadzi za chombo sizinalinganizidwe molongosoka, kuwongolera kayendedwe koyenera sikungapangidwe. Mofananamo, ngati titi tisunge miyoyo yathu panjira yake, tifunikira chitsogozo cholongosoka cha Mawu a Mulungu, Baibulo. ‘Lemba liri lonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero.’ (2 Timoteo 3:16) Mawu ouziridwa amenewo amapereka miyezo ya Mulungu ya mayendedwe ndi kalingaliridwe. Kuwaŵerenga mokhazikika nkofunika kwambiri kuti muyende ‘m’mabande a chilungamo.’—Salmo 23:3.
Chilangizo chowonjezereka chimachokera ku kagulu ka “kapolo wokhulupirika ndi wanzeru” ka Akristu odzozedwa. Awa akhala akuthandizidwa ndi mzimu wa Yehova kumvetsetsa chifuniro chake mopita patsogolo. (Mateyu 24:45-47; Miyambo 4:18) Chotero, pamene chilangizo chibwera kuchokera ku gulu la Yehova, tingangonjere mwanzeru, tikudziŵa bwino lomwe kuti Yehova adzatitsogolera kokha m’njira imene idzatidzetsera phindu losatha.—Yesaya 48:17.
Komabe, panthaŵi zina, timafunikira chithandizo chaumwini kuti tikhalebe panjira. Paulo analangiza pa Agalatiya 6:1 kuti: ‘Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze woteroyo mu mzimu wachifatso.’ Akulu ndi atumiki otumikira ali pakati pa okhala ndi ziyeneretso zoterozo. Kaŵirikaŵiri iwo adzatitchulira mwachindunji mbali zina zimene tifunikira kuwongokera.
Kuyesayesa Nkofunikira
Sikuli kosavuta nthaŵi zonse kupanga masinthidwe ofunikira m’miyoyo yathu. Kachiŵirinso, tamlingalirani Petro. Wobadwa Myuda, Petro anakula akukhala ndi phande m’lingaliro lofalikira latsankho kwa anthu amafuko ena. Monga momwe anauzira Korneliyo Wakunja kuti: “Mudziwa inu nokha kuti sikuloledwa kwa munthu Myuda adziphatike kapena kudza kwa munthu wa mtundu wina.” Komabe, atazindikira kuti chinali chifuniro cha Mulungu kuti agaŵane chowonadi Chachikristu ndi mwamunayu ndi banja lake, Petro anamaliza kuti: ‘Zowona ndizindikira kuti Mulungu alibe tsankho; koma m’mitundu yonse, wakumuwopa iye ndi wakuchita chilungamo alandiridwa naye.’—Machitidwe 10:28, 34, 35.
Petro adapanga masinthidwe odabwitsa m’kulingalira kwake ndi mkhalidwe kulinga kwa mafuko ena! Koma mwachiwonekere panali kufunikira kwakuti iye apitirize kukhala wowongolereka mwanjirayi, popeza kuti zaka zoŵerengeka pambuyo pake, Petro anagonjera ku chipsinjo cha anzake ndikuyamba kunyalanyaza okhulupirira Akunja. Mtumwi Paulo anafunikira kumdzudzula, mwamawu amphamvu ndithu kumthandiza kuwongolera kulingalira kwake mowonjezereka!—Agalatiya 2:11-14.
Mofananamo lerolino, Mkristu angakhale anakulira mumkhalidwe wakusankhana fuko. Atabwera m’chowonadi, angazindikire kuti Mulungu alibe tsankho komabe iye akumamatirabe ku malingaliro akusankhana fuko. Ngakhale kuti samada afuko lina, iye angawalingalire kukhala ndi mikhalidwe yosafunikira chifukwa cha mwambo wa fuko lawo. Angakhale akuyesa kuleza mtima kwawo mwa njerengo zoseka fuko kapena mawu amene amakumbutsa fuko, kapena kusiyana kwa mafuko. Iye angakane ngakhale chilangizo chauzimu chochokera kwa Mkristu mnzake amene, chifukwa chokhala wosaphunzira kapena kusoŵa mwaŵi wakutiwakuti wazakakhalidwe, angalephere kulankhula malingaliro ake mumkhalidwe winawake. Mwachiwonekere, kungafunikiritse kuyesayesa kwamphamvu kuti munthu woteroyo asinthe kalingaliridwe kake kugwirizana ndi ka Yehova!a
Koma ngakhale ngati nkhani ingakhale tsankho laufuko, kukondetsa zinthu zakuthupi, kudziloŵetsa m’zamayanjano pasukulu ndi pantchito, kapena kufunika kwa kupezeka ku misonkhano Yachikristu, tiyenera kutsatira chitsogozo choperekedwa kupyolera m’Mawu a Mulungu ndi gulu lake. Sitiyenera konse kulingalira kuti uphungu Wamalemba woyenera sukugwira ntchito kwa ife ndi kuunyalanyaza. Kumbukirani kuti Aisrayeli osakhulupirika anati: “Njira ya [Yehova, NW] njosayenera.” Kodi sindife amene tiyenera kuwongokerera ku njira za Yehova?—Ezekieli 18:25.
Tikusangalala kuti Yehova akukondwera ndi njira imene tikuyendera pamaso pake, akupereka kuwongolera kosalekeza kaamba ka anthu ake. Ziri monga momwe Yesaya analosera kuti: “Ndipo makutu ako adzamva mau kumbuyo kwa iwe akuti, Njira ndi iyi, yendani inu m’menemo: potembenukira inu kulamanja, ndi potembenukira kulamanzere.” Tikhaletu atcheru ku chilangizo chachikondi chochokera kwa Yehova ndi kukhala ‘okonzekera kumvera.’ (Yesaya 30:21; Yakobo 3:17, NW) Inde, tipitirizetu kukhala owongolereka kotero kuti njira yathu ititsogolere ku chonulirapo cha umuyaya m’chiyanjo cha Mulungu!
[Mawu a M’munsi]
a Onani nkhani pa tsankho yopezeka m’kope la August 8, 1985, la magazini athu ena a Galamukani! Onaninso Nsanja ya Olonda ya May 15, 1988, masamba 10-20.