Cisanu, April 17
Musalole kuti aliyense akusoceletseni mwa njila iliyonse.—2 Ates. 2:3.
Tiphunzilapo ciyani pa mawu amene mtumwi Paulo analembela Atesalonika? Tikamva nkhani inayake imene sigwilizana na zimene tinaphunzila m’Baibo, kapena tikamva nkhani inayake yocititsa cidwi koma yodabwitsa, tiyenela kukhala osamala. Mu ulamulilo wakale wa Soviet Union, adani athu anapatsa abale kalata yooneka ngati yacokela ku likulu lathu. Kalata imeneyo inalimbikitsa abale na alongo kuti adzipatule ku gulu la Yehova na kupanga gulu lawo lodziimila palokha. Kalata imeneyo inali kuoneka ngati yacokeladi kulikulu lathu. Koma abale na alongo okhulupilika sanapusitsidwe. Iwo anazindikila kuti zimene kalatayo inakamba zinali zosiyana na zimene anaphunzila. Masiku anonso, adani a coonadi amaseŵenzetsa njila zamakono na colinga cakuti atisokoneze na kubweletsa magaŵano pakati pathu. M’malo molola “kuti wina aliyense asinthe maganizo” athu mosavuta, tiyeni tidziteteze mwa kuganizilapo mozama ngati zimene tamva kapena kuŵelengazo zigwilizana na coonadi cimene tinaphunzila kale.—2 Ates. 2:2; 1 Yoh. 4:1. w24.07 12 ¶14-15
Ciwelu, April 18
Wina akacita chimo, tili ndi wotithandiza.—1 Yoh. 2:1.
Cisankho cofunika kopambana cimene munthu aliyense angapange ni cisankho codzipatulila kwa Yehova na kukhala m’banja la alambili ake. Yehova amafuna kuti munthu aliyense apange cisankho cimeneci. N’cifukwa ciyani? Iye amafuna kuti anthu akhale paubwenzi wabwino na iye, komanso kuti akhale na moyo kwamuyaya. (Deut. 30:19, 20; Agal. 6:7, 8) Komabe, Yehova sakakamiza munthu aliyense kuti am’tumikile. Iye amalola munthu aliyense kupanga cisankho com’tumikila kapena ayi. N’ciyani cimacitika ngati Mkhristu wobatizika waphwanya malamulo a Mulungu na kucita chimo lalikulu? Ngati munthuyo si wolapa, ayenela kucotsedwa mumpingo. (1 Akor. 5:13) Ngakhale n’telo, Yehova amakhala wofunitsitsa kuti munthuyo alape na kubwelela kwa iye. Ni iko komwe, ici ndiye cifukwa cacikulu cimene Yehova anapelekela dipo. Colingaco cinali cakuti zizikhala zotheka munthu wocimwa akalapa kukhululukidwa macimo ake. Mulungu wathu wacikondi amapempha ocimwa kuti alape.—Zek. 1:3; Aroma 2:4; Yak. 4:8. w24.08 14 ¶1-2
Sondo, April 19
Mtima wako ukakhala wanzelu, ndithu mtima wanga udzasangalala.—Miy. 23:15.
Panthawi imene mtumwi Yohane analemba za cimwemwe cimene cimabwela munthu akakhala womvela kwa Mulungu. Panthawiyo, anthu ena anali kufalitsa ziphunzitso zabodza na kubweletsa magaŵano mumpingo. Ngakhale n’telo, ena anali ‘kuyendabe m’coonadi.’ Iwo anali kumvela Yehova ndipo anali “kuyenda motsatila malamulo ake.” (2 Yoh. 4, 6) Zimene Akhristu okhulupilikawo anacita, zinasangalatsa Yohane komanso Yehova. (Miy. 27:11) Kodi tiphunzilapo ciyani? Kukhala wokhulupilika kumabweletsa cimwemwe. (1 Yoh. 5:3) Mwacitsanzo, timakhala acimwemwe podziŵa kuti timakondweletsa Yehova. Yehova amakondwela tikakaniza mayeselo a dzikoli na kutsatila malamulo ake. Nawonso angelo kumwamba amasangalala. (Luka 15:10) Nafenso timakhala acimwemwe tikaona Mkhristu mnzathu akukhalabe wokhulupilika. (2 Ates. 1:4) Ndipo dongosolo loipali likadzapita, tidzakhala acimwemwe podziŵa kuti tinakhala okhulupilika kwa Yehova m’dziko lolamulidwa na Satana. w24.11 12 ¶17-18