AUGUST 10-16, 2026
NYIMBO NA. 122 Khalani Olimba Komanso Osasunthika
Tingatani Kuti Tikhalebe Okhulupirika Tikakumana ndi Zinthu Zoyesa Chikhulupiriro?
“Ambuye, tingapitenso kwa ndani? Inu ndi amene muli ndi mawu othandiza munthu kuti adzapeze moyo wosatha.”—YOH. 6:68.
ZIMENE TIPHUNZIRE
Tiona kuti n’zotheka kukhalabe okhulupirika kwa Yehova kaya takumana ndi mayesero otani.
1-2. Kodi chinachitika n’chiyani pamene Yesu ankaphunzitsa ku Kaperenao?
TSIKU lina Yesu akuphunzitsa gulu la anthu ku Kaperenao, anawauza kuti: “Mukapanda kudya mnofu wa Mwana wa munthu ndi kumwa magazi ake, simudzapeza moyo. Aliyense amene amadya mnofu wanga ndi kumwa magazi anga adzapeza moyo wosatha ndipo ndidzamuukitsa pa tsiku lomaliza.” (Yoh. 6:53, 54) Ambiri mwa ophunzira ake sanasangalale ndi zimene iye ananena. Iwo anati: “Mawu amenewa ndi ozunguza. Ndi ndani angamvetsere zimenezi?”—Yoh. 6:60.
2 Anthu omwe anakhumudwa kwambiri ndi mawu a Yesuwa anasiya kumutsatira. Sikuti anachita zimenezi chifukwa choti sankamukhulupirira. Tikutero chifukwa izi zisanachitike, anthu ena kuphatikizapo ophunzira a Yesu, anagoma ndi zimene Yesuyo anachita, moti ananena kuti: “Mosakayika uyu ndi mneneri uja amene anati adzabwera padziko.” (Yoh. 6:14) Apa n’zoonekeratu kuti ophunzirawa ankamukhulupirira ndithu. Koma chikhulupiriro chawo chitayesedwa anasiya kukhala okhulupirika.
3. Kodi atumwi anatani atamva zimene Yesu ananena, nanga n’chifukwa chiyani? (Onaninso chithunzi.)
3 Atumwi anachita zinthu mosiyana ndi anthu onse. Yesu atawafunsa ngati nawonso akufuna kumusiya, Petulo anayankha kuti: “Ambuye, tingapitenso kwa ndani? Inu ndi amene muli ndi mawu othandiza munthu kuti adzapeze moyo wosatha. Ife takhulupirira ndipo tadziwa kuti inu ndinu Woyera amene Mulungu anamutumiza.” (Yoh. 6:68, 69) Apa Petulo sananene kuti iyeyo ndi atumwi anzakewo anali atamvetsa zimene Yesu ankatanthauza pamene anawauza kuti adye mnofu wake komanso amwe magazi ake. Ngakhale kuti sankamvetsa zonse pa nthawiyo, anasankha kukhalabe okhulupirika kwa Yesu. Anachita zimenezi chifukwa ankakhulupirira mfundo yosatsutsika ya choonadi yakuti Yesu ndi “Khristu wa Mulungu.”—Luka 9:20, 35.
Ngakhale kuti ophunzira ambiri a Yesu anamusiya, Petulo ndi atumwi ena anakhalabe okhulupirika kwa iye (Onani ndime 3)
4. Kodi tingakumane ndi mayesero ati?
4 Pali zinthu zambiri zimene zingayese kukhulupirika kwathu. Mwachitsanzo, kodi timatani tikamva za kusintha pa nkhani ya mmene timamvera mfundo inayake ya m’Baibulo kapena mmene tizigwirira ntchito yolalikira? Nanga kodi timatani ngati tikuvutika kumvetsa chifukwa chake Yehova walola kuti tikumane ndi mavuto enaake? Chikhulupiriro chathu chikhozanso kuyesedwa ngati Mkhristu mnzathu watikhumudwitsa kapena ngati munthu wina amene timamulemekeza watichitira zinthu zopanda chilungamo.
5. N’chifukwa chiyani timayenera kulimbitsa chikhulupiriro chathu? Perekani chitsanzo. (Akolose 1:23)
5 Kuti timvetse chifukwa chake tiyenera kukhala ndi maziko olimba a chikhulupiriro chathu, tiyeni tiganizire za nyumba yomwe inamangidwa kumalo amene kumakonda kuchitika zivomerezi. Kuti nyumbayo isagwe imafunika kukhala ndi maziko olimba. Mofanana ndi zimenezi, kuti ifenso tipitirizebe kukhala okhulupirika tikakumana ndi zinthu zoyesa chikhulupiriro zomwe tazitchula m’ndime yapitayi, chikhulupiriro chathu chiyenera kukhala ndi maziko olimba. Choncho tikamapitiriza kulimbitsa chikhulupiriro chathu, timakhala osasunthika komanso okhulupirika kwa Yehova pamene tikukumana ndi mayesero.—1 Akor. 15:58; werengani Akolose 1:23.
6. Kodi n’chiyani chinathandiza atumwi kukhalabe okhulupirika kwa Yesu anthu ambiri atamusiya?
6 Atumwi ankakhulupirira kuti Yehova ndi woyenera kumulambira chifukwa ndi amene analenga zinthu zonse. Ankakhulupiriranso kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu amene ali ndi “mawu othandiza munthu kuti adzapeze moyo wosatha,” komanso kuti Yehova ndi amene ankamutsogolera. M’malo mokambirana zinthu zosiyanasiyana zomwe zingayese chikhulupiriro chathu, tiyeni tikambirane mfundo zitatu za choonadi zomwe zingatithandize kukhalabe olimba kaya takumana ndi mayesero otani. Mfundo zake ndi izi: (1) Yehova ndi Mlengi wa zinthu zonse, (2) Baibulo linauziridwa ndi Yehova komanso (3) Yehova akutsogolera anthu ake masiku ano. Tikamakhulupirira ndi mtima wonse kuti mfundo zitatuzi ndi zoona, timakhalabe okhulupirika pamene tikukumana ndi mayesero.
YEHOVA NDI MLENGI
7. Kodi lemba la Chivumbulutso 4:11 limatiuza chiyani zokhudza Yehova, nanga n’chiyani chingachitike tikakumana ndi zinthu zoyesa chikhulupiriro chathu?
7 Werengani Chivumbulutso 4:11. Lembali limatikumbutsa kuti Yehova ndi amene analenga zinthu zonse. Mfundo imeneyi imamuchititsa kuti akhale woyenera kuti tizimulambira. Tikamaganizira za mphamvu zake zodabwitsa, sitikayikira kuti akhoza kutipulumutsa pa mayesero athu onse. Komabe, Satana amafalitsa mabodza amene amachititsa anthu m’dzikoli kukayikira zoti Mulungu aliko. Ngakhale asayansi ena amanena kuti moyo unangokhalapo wokha. Choncho ngati sitikhulupirira ndi mtima wonse kuti Yehova ndi Mlengi komanso kuti amatikonda, tikhoza kuyamba kukayikira kuti alipo komanso kuti angatithandize pamene takumana ndi zinthu zoyesa chikhulupiro chathu.—Aheb. 11:6.
8-9. Kodi muyenera kutani ngati mwayamba kukayikira zoti Yehova ndi Mlengi? (Onaninso chithunzi.)
8 Ngati mwayamba kukayikira kuti Yehova ndi Mlengi, chitanipo kanthu mwamsanga. Muzifufuza mosamala m’mabuku athu mfundo zimene zimatipatsa umboni wosatsutsika wakuti Yehova ndi amene analenga zinthu zonse. Mungapeze mfundo zomwe zingalimbitse chikhulupiriro chanu pa nkhaniyi m’kabuku kakuti, Kodi Zamoyo Zinachita Kulengedwa? komanso kakuti, Mmene Moyo Unayambira—Mafunso 5 Ofunika Kwambiri. Mungapezenso umboni wina munkhani zakuti “Kodi Zinangochitika Zokha?” pa jw.org. Mlongo wina wachitsikana wa ku United States dzina lake Jessica ananena kuti: “Nditawerenga kabuku kakuti Mmene Moyo Unayambira, ndinayamba kukhulupirira kwambiri kuti pali winawake wanzeru amene analenga zinthu zonse. Ndinkazidziwa kale mfundozi koma nditawerenga kabukuka ndinapeza umboni wamphamvu wakuti kuli Mlengi.” Komanso anthu ambiri anapeza mfundo zothandiza atawerenga buku la Chingelezi lakuti, Is There a Creator Who Cares About You? N’kutheka kuti munaliwerengapo kale komabe mungachite bwino mutaliwerenganso.
9 Ulendo wotsatira mukamadzawerenga Baibulo panokha, bwanji osakonza zoti mudzafufuze mfundo zokutsimikizirani kuti Mulungu alipo? Mfundo zomwe mungadzapezezo zidzakuthandizani kuti muzikhulupirira kwambiri kuti Yehova alipo komanso kumvetsa bwino zokhudza makhalidwe ake. (Aroma 1:20) Kuwonjezera pamenepa, mudzathanso kugwiritsa ntchito mfundozi pothandiza ena amene amakayikira kuti Mulungu alipo. Mfundo yaikulu ndi yakuti: Yehova watipatsa umboni wokwanira wakuti iyeyo ndi Mlengi wathu.
Nebula: IAC/RGO/David Malin Images; fish and car: Mercedes-Benz USA; plane: Kristen Bartlett/University of Florida
Ngati munawerengapo kale kabuku kakuti Kodi Zamoyo Zinachita Kulengedwa? mungachite bwino kukawerenganso (Onani ndime 8)
BAIBULO LINAUZIRIDWA NDI YEHOVA
10. N’chifukwa chiyani timaona kuti Baibulo ndi lofunika? (2 Timoteyo 3:16, 17)
10 Werengani 2 Timoteyo 3:16, 17. M’Baibulo muli uthenga umene Yehova analembera anthu. Limayankha mafunso ofunika kwambiri okhudza moyo, limatiuza cholinga cha Yehova komanso zimene amafuna kuti anthufe tizichita. Timakhulupirira kuti Yehova ndi amene analemba Baibulo ndipo timaona kuti bukuli ndi lofunika kwambiri pa moyo wathu. Timayesetsa kuti timvetse mfundo zake komanso tizizigwiritsa ntchito pa moyo wathu.
11. N’chiyani chimakutsimikizirani kuti Baibulo linauziridwa ndi Mulungu?
11 N’chiyani chimatitsimikizira kuti Baibulo linauziridwa ndi Yehova? Pali zinthu zingapo. Limanena zolondola pa nkhani yokhudza mbiri yakale. (Luka 3:1, 2) Limanenanso zolondola pa nkhani ya chilengedwechi. (Yobu 26:7) Baibulo ndi buku limene lafalitsidwa kwambiri kuposa mabuku onse ngakhale kuti Satana wakhala akuyesetsa kuti aliwononge. Ngakhale kuti linalembedwa ndi amuna 40 osiyanasiyana komanso linatenga zaka zoposa 1,600 likulembedwa, uthenga wake ndi wogwirizana. Lilinso ndi malangizo amene akuthandiza anthu mamiliyoni pa moyo wawo wa tsiku ndi tsiku. (Miy. 13:20; 15:21; Mat. 7:12) Ndipotu maulosi ambiri a m’Baibulo anakwaniritsidwa, zomwe zimangotitsimikizira kuti bukuli ndi lodalirika. (Yos. 23:14) Umenewutu ndi umboni wakuti Baibulo linauziridwa ndi Mulungu.
12. Kodi tiyenera kuchita chiyani ngati tayamba kukayikira zoti Baibulo linauziridwa ndi Mulungu?
12 Kodi tiyenera kuchita chiyani ngati tayamba kukayikira kuti Baibulo linauziridwa ndi Mulungu? Tiyenera kuipempherera nkhaniyi komanso kuchita zinthu mogwirizana ndi pemphero lathulo. Tamvani zimene mnyamata wina yemwe anakulira m’banja la Mboni dzina lake Jordan ananena. Iye anati: “Mwachibadwa sindimangofulumira kukhulupirira zilizonse zimene ndauzidwa, ndimafuna ndiziganizire kaye pandekha. Kunena moona mtima nthawi zina ndimakayikira zinthu zina koma ndikayamba kukhala ndi maganizo okayikira, ndimafufuza mayankho a mafunso anga m’mabuku athu n’cholinga choti ndisiye kukayikirako.” Tikamapitiriza kupeza umboni wotitsimikizira kuti Yehova ndi amene analemba Baibulo, chikhulupiriro chathu chimalimba kwambiri.—1 Akor. 3:12, 13.
YEHOVA AKUTSOGOLERA ANTHU AKE MASIKU ANO
13. Kodi tizitani tikayamba kukayikira kuti a Mboni za Yehova ndi anthu a Mulungu masiku ano?
13 Tikayamba kukayikira zoti a Mboni za Yehova ndi anthu amene Yehova akuwatsogolera masiku ano, tizichitapo kanthu mwamsanga. Tingadzifunse mafunso ngati awa: ‘Kodi ndi anthu ati amene amayesetsa kutsatira mfundo za m’Baibulo pa moyo wawo? Ndi gulu liti limene zonse zimene limakhulupirira zimachokera m’Baibulo?’ (2 Tim. 4:3, 4) ‘Nanga ndi ndani amene amachita zimene Mulungu amafuna masiku ano?’—Mat. 7:20, 21.
14. Kodi Mulungu akugwiritsa ntchito bwanji a Mboni za Yehova pokwaniritsa zomwe zili pa Mateyu 24:14?
14 Pa nkhani ya anthu amene akuchita zimene Mulungu amafuna masiku ano, tingadzifunse kuti, ‘Ndi ndani amene akugwira ntchito yolalikira imene Yesu ananeneratu kuti idzachitika m’masiku otsiriza?’ (Mat. 24:14) Yankho ndi lodziwikiratu. Mulungu akugwiritsa ntchito anthu ake omwe ndi a Mboni za Yehova kuti azigwira ntchito yolalikira. Ndi ife tokha amene tikulalikira uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu m’mayiko oposa 240. Ndipo takhala tikugwira ntchitoyi kwa zaka zoposa 100. Nthawi zonse timaona kuti ntchito yolalikira komanso kuphunzitsa anthu Mawu a Mulungu ndi yofunika kwambiri.—Mat. 28:19, 20.
15. Kodi a Mboni za Yehova amathandiza bwanji poyeretsa dzina la Mulungu masiku ano? (Mateyu 6:9; Yesaya 43:10)
15 Werengani Mateyu 6:9 ndi Yesaya 43:10. Timadziwika ndi dzina lenileni la Mulungu lakuti Yehova ndipo timanyadira kutchedwa kuti a Mboni za Yehova. Anthu ambiri m’dzikoli sadziwa kuti dzina la Mulungu ndi Yehova. Koma ife tinayesetsa kubwezeretsa dzinali m’malo ake onse m’Baibulo. Dzinali limapezeka maulendo oposa 7,000 mu Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika.
16. N’chifukwa chiyani tinganene kuti a Mboni za Yehova amamvera lamulo la pa Yohane 13:34, 35? (Onaninso chithunzi.)
16 Werengani Yohane 13:34, 35. Ubale wathu wapadziko lonse ndi chinthu chodabwitsa kwambiri chifukwa timakondana komanso kugwirizana zomwe ndi zosiyana kwambiri ndi anthu a m’dzikoli. Ngakhale kuti timachokera m’mayiko osiyanasiyana, tili ndi zikhalidwe zosiyanasiyana, komanso tinaleredwa mosiyanasiyana, timayesetsa kukhala mwamtendere ndipo timakondana. Mwachitsanzo, kodi munasonkhanapo ndi mpingo wina mutapita kudera linalake? Ngati ndi choncho, mwina munaona kuti abale ndi alongo amakondana komanso kugwirizana. Izi zikusonyezeratu kuti Yehova akugwiritsa ntchito Mboni zake masiku ano kuti zikwaniritse cholinga chake. Kukumbukira zimenezi kungatithandize kuti tizikhalabe okhulupirika kwa Yehova tikakumana ndi zinthu zoyesa chikhulupiriro chathu.
Ubale wathu wapadziko lonse ndi chinthu chodabwitsa kwambiri chifukwa timakondana komanso kugwirizana (Onani ndime 16)a
MUSASIYE YEHOVA
17-18. Kodi ndi mavuto ati amene tingakumane nawo, nanga sitikayikira za chiyani?
17 Tikukhala m’nthawi yapadera komanso yovuta, choncho zinthu zina zizikhala zovuta m’masiku otsiriza ano. (2 Tim. 3:1, 13) Tingamade nkhawa ndi zinthu zina zomwe zikuchitika. Gulu la Yehova lingasankhe zinthu zomwe zingamativute kuti tizimvetse bwinobwino. M’bale kapena mlongo akhoza kutikhumudwitsa kapenanso tingamaone ngati sanatimvetse. Tikhoza kumavutika kupeza njira yothetsera vuto limene takumana nalolo kapenanso sitingathe kumvetsa chifukwa chake takumana ndi zinazake.
18 Ngakhale kuti tingakhumudwe ndi zimene zatichitikira, tingakhalebe okhulupirika kwa Yehova ngati timakhulupirira mfundo yakuti iye ndi Mlengi, Baibulo ndi Mawu ake komanso kuti a Mboni za Yehova ndi anthu ake. Mogwirizana ndi zimene Petulo anauza Yesu, ifenso tikhoza kuuza Yehova kuti: “Tingapitenso kwa ndani? Inu ndi amene muli ndi mawu othandiza munthu kuti adzapeze moyo wosatha.”
NYIMBO NA. 123 Tizigonjera Mulungu Mokhulupirika
a MAWU OFOTOKOZERA CHITHUNZI: Mwana ndi mayi ake akwera basi ndipo akusangalala kuona a Mboni anzawo akulalikira.