‘Kulalikira Uthenga Wabwino’ Kudzera mu Ntchito ya Mayanjano
KUO TUNG, mwamuna wachichepere wa chiBudda kuchokera ku Hong Kong, analandira maphunziro a pa koleji. Hsiu Ying, mayi wa ku Taiwan, anapeza thandizo lofunikira kwambiri kaamba ka matenda a kayakaya a mwana wake wamwamuna. Kodi ndi chinthu chofanana chiti chimene zochitika ziwiri zooneka zosiyana izi ziri nacho?
Maphunziro a pa koleji mwachionekere akanakhala osalingalirika kaamba ka Kuo Tung. Koma kudzera ku tchalitchi chomwe iye ali membala, zitseko zinatsegulidwa kaamba ka iye. Mofananamo, njira yakachiritsidwe yocholowanacholowana yomwe inafunikira kwa mwana wamwamuna wa Hsiu Ying inalipo kokha ku chipatala cha tchalitchi chomwe chinali mudera lake. Kachiwirinso, kudzera muchigwirizano ndi tchalitchi, vutolo linathetsedwa.
Nkhani za Kuo Tung ndi Hsiu Ying ziri mosakaikira zosadabwitsa. Zikwi za anthu mu maiko okwera kumene zakokedwera ku masukulu, zipatala, nyumba za ana amasiye, ndi malo ena ophunzirirako amayanjano otsogozedwa ndi matchalitchi. Mu njirayi apeza mapindu akuthupi okulira kaamba ka iwo eni. Ndipo mwanjirayo, mwakudziphatikiza ku tchalitchi ambiri a iwo athandiza kukulitsa chiwerengero cha mamembala a tchalitchi.
Chizolowezi Chokhala ndi Mbiri Yakale
Masukulu ndi zipatala za tchalitchi, m’chenicheni, siziri zachilendo. Kwenikweni, kuyambira mu masiku oyambirira pamene amishonare anali kutumizidwa ku maiko amene ena anawatcha kukhala maiko andewu akunja, masukulu ndi zipatala zinaonedwa kukhala njira yokhutiritsa kwambiri ya kutsegulira magawo atsopano ndi kupeza chikhulupiriro ndi ubwenzi wa anthu a kumaloko.
Mwa chitsanzo, polongosola mikhalidwe muIndia kumayambiriro kwa zana la 19, bukhu lochedwa Nineteen Centuries of Missions (1899) linanena kuti: “Amishonale sali kweni kweni, o lowetsedwa mu ntchito ya ulaliki koma iwo akugwiranso ntchito ya chipambano choonekera mu maphunziro, mankhwala ndi ntchito ya zenana [chipinda cha akazi m’nyumba ya amwenye].” Choturukapo chake? “Mishoni iri yonse iri ndi sukulu ya patsiku, ndi zochitachita ndi sukulu zogonera konko, sukulu yapamwamba kapena koleji, ndipo chifupifupi mu mbali iriyonse, sukulu ya maphunziro a za umulungu.”
Kuthira ndemanga pa ntchito ya kuchiritsa mu “bizinesi ya umishonale,” bukhulo likupitiriza kunena kuti: “Sing’anga nthawi zonse ali wolandiridwa, ndipo mpumulo woperekedwa mu kuvutika kwa kuthupi sumapereka kokha chidaliro mwa sing’anga, koma kawiri kawiri chimatsatiridwa ndi chikhulupiriro muchipembedzo chimene iye amaphunzitsa. Midzi yonse mochulukira imatsogoleredwa monga choturukapo cha chithandizo cha mankhwala, kutaya kulambira mafano ndi kula ndira malangizo Achikristu.”
Chomwe chinali choona mu India chinakhalanso choona mu maiko ena a ku m’Mawa, South America, ndi Afirika. Lingaliro lakulalikira uthenga wabwino kudzera mu mayanjano lakhala likupita patsogolo. Masosaite a umishonale a ku Europe ndi Amereka, ponse pawiri a Katolika ndi Protesitanti, anatumiza ogwira ntchito m’madera amenewa ndi kukhazikitsa mamishoni awo limodzi ndi masukulu, zipatala, ndi malo ophunzitsira ena. Zambiri za izi zikukhala zachipambano m’kukokera anthu a kumaloko ku ntchito za mayanjano zotero ndipo mwamsanga akumabwera kukhala mbali ya ntchito ya umishonale ya maiko akunja yotsogozedwa ndi tchalitchi.
Mkati mwa zaka zokhazikitsidwa zotsogozedwa ndi tchalitchi zimenezi zakula kutenga malo ofunika kwambiri m’malo a midzi yaku maloko. Masukulu awo ndi mayunivesite awo kawirikawiri ali onyadirika ndipo ali malo ophunzirira a maphunziro apamwamba omwe aliyense amakhumbira. Mwachisawawa, zipatala zawo ziri ndi zogwiritsira ntchito zabwino koposa ndipo zamakono kwambiri. Ndipo mu madera ochuluka, kumene boma liri lopanikizika kaamba ka mavuto amayanjano okulira, iwo ali olandiridwa kwambiri, ndipo mwina mwake ali opatsidwa ulemu.
Palibe chikaikiro chiri chonse chakuti mautumiki operekedwa kudzera mu maprogramu oterowo anaturukira ku ubwino kaamba ka midzi yomwe inatumikiridwa. Masukulu otsogozedwa ndi tchalitchi limodzi ndi mayunivesite apereka kwenikweni kwa zikwi za ophunzira ambiri maphunziro omwe mwina mwake sakanakhala nawo. Zipatala zotero ndi mautumiki a zaumoyo abweretsa mpumulo kwa anthu osawerengeka mu madera akutali ndi madera obwerera m’mbuyo. Ntchito ya umunthu ya Albert Schweitzer ndi “Mayi” Teresa, mwachitsanzo, ziri zodziwika kwambiri kwa anthu onse ndipo onse awiri anapeza mphoto ya Nobel peace prize. (Mphatso Yaochita Zotchuka za Pachaka)
Ku mbali ina, wina ayenera kufunsa: Kodi uthenga wabwino wa mayanjano wachifikiradi cholinga chake? Kodi chapanga Akristu enieni a awo omwe apindula kuchokera ku ntchito zawo zaufulu? Kodi chapatsa anthu chikhulupiriro chenicheni ndi chiyembekezo? Ndipo chofunika kwambiri, tiyenera kufunsa: Kodi ichi ndi chimene Yesu anali nacho m’maganizo pamene iye anatumiza otsatira ache ‘kulalikira uthenga wabwino mu dziko lonse lapansi’?—Mateyu 24:14, King James Version.