MUNTHU WOTCHULIDWA M’BAIBULO
Muzikhala Olimba Mtima Komanso Okhulupirika Ngati Benaya
Benaya anali msilikali wolimba mtima yemwe anatumikira Mfumu Davide komanso Solomo. Ngakhale kuti anali mwana wa wansembe ndipo sankafunika kumenya nkhondo, iye ankamenya nawo nkhondo za Yehova ndipo anasonyeza kulimba mtima kwambiri. Mwachitsanzo, Benaya anapha mkango m’chitsime chopanda madzi komanso munthu yemwe anali wamkulu modabwitsa. Davide ankakhulupirira kwambiri Benaya moti anamuika kukhala mkulu wa asilikali omulondera.—2 Sam. 23:20-23.
Benaya anakhalabe wokhulupirika kwa Davide pamene Abisalomu komanso Adoniya anaukira ulamuliro wake. (2 Sam. 8:18; 15:18; 1 Maf. 1:8) Davide atakalamba, Benaya anathandiza Solomo kukhala mfumu. (1 Maf. 1:32-40) Benaya anali wokhulupirika kwa Yehova komanso kwa mafumu amene Yehovayo anawasankha, ngakhale pamene anthu ena sanali okhulupirika.
Ifenso timafunika kukhala olimba mtima kuti tithe kulimbana ndi mdani wathu wamkulu Satana ndiponso amene ali kumbali yake. Ndipo tiyenera kutsimikiza mtima kuti tipitiriza kutsatira mfundo za Yehova. (Aef. 6:11; 1 Pet. 5:8, 9) Ngakhale pamene ena asankha kusiya Yehova, timakhalabe okhulupirika kwa iye ndipo sitikayikira kuti adzatidalitsa.—2 Sam. 22:26.