Ndandanda ya Mlungu wa December 1
MLUNGU WOYAMBIRA DECEMBER 1
Nyimbo Na. 105 ndi Pemphero
Phunziro la Baibulo la Mpingo:
cl mutu 5 ndime 1-8 (Mph. 30)
Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Deuteronomo 32-34 (Mph. 10)
Na. 1: Deuteronomo 32:22-35 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: Munthu Akafa, Mzimu Wake Kapena Kuti Moyo Wake Supitirizanso Kukhala Ndi Moyo—rs tsa. 297 ndime 1–tsa. 299 ndime 3 (Mph. 5)
Na. 3: Kuchita Chigololo Ndi Kuchimwira Mulungu—lv tsa. 128-129 ndime 16-19 (Mph. 5)
Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 10: Zimene Munganene Pogawira Magazini a December. Nkhani yokambirana. Chitani zitsanzo zitatu zomwe zili patsamba lino. Mukamaliza kuchita chitsanzo chilichonse, pemphani omvera kuti afotokoze chifukwa chake anthu ambiri a m’gawo lanu angakhale ndi chidwi ndi nkhanizi.
Mph. 10: Zofunika pampingo.
Mph. 10: Kodi Tinachita Zotani? Nkhani yokambirana. Pemphani omvera kuti afotokoze phindu lomwe apeza pogwiritsa ntchito malangizo a m’nkhani yakuti, “Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Muzisonyeza Chidwi Munthu Amene Mukumulalikira.” Apempheninso kuti afotokoze zinthu zosangalatsa zomwe zinachitika pomwe ankagwiritsa ntchito mfundo za m’nkhaniyi.
Nyimbo Na. 119 ndi Pemphero