Ndandanda ya Mlungu wa April 14
MLUNGU WOYAMBIRA APRIL 14
Nyimbo Na. 68 ndi Pemphero
Phunziro la Baibulo la Mpingo:
jr mutu 10 ndime 8-13 (Mph. 30)
Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Ekisodo 11-14 (Mph. 10)
Na. 1: Ekisodo 12:37-51 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: Zinthu Zina Zimene Zimasonyeza Kukhalapo kwa Khristu—rs tsa. 165 ndime 1-5 (Mph. 5)
Na. 3: Kodi Satana Amafalitsa Mabodza Ati Okhudza Machimo Akuluakulu?—lv tsa. 164 ndime 1-4 (Mph. 5)
Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 15: Werengani Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2014. Nkhani yokambirana. Kambiranani “Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira.” Muuziretu ofalitsa ena kuti adzafotokoze zochitika zochititsa chidwi za mu Buku Lapachaka limeneli, zomwe n’zolimbikitsa kwambiri. Pemphani omvera kuti afotokoze ziwerengero zochititsa chidwi zomwe zikupezeka m’lipoti lapadziko lonse la Mboni za Yehova. Pomaliza, limbikitsani anthu onse kuti awerenge Buku Lapachaka limeneli.
Mph. 15: “Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Muzithandiza Mnzanu Amene Mwayenda Naye.” Nkhani yokambirana. Chitani zitsanzo ziwiri zachidule zosonyeza munthu amene wayenda ndi mnzake mu utumiki koma sakumuthandiza. Pamapeto pa chitsanzo chilichonse, pemphani omvera kuti afotokoze zimene munthuyo anayenera kuchita.
Nyimbo Na. 45 ndi Pemphero