Ndandanda ya Mlungu wa January 13
MLUNGU WOYAMBIRA JANUARY 13
Nyimbo Na. 62 ndi Pemphero
Phunziro la Baibulo la Mpingo:
jr mutu 6 ndime 7-12 ndi bokosi patsamba 73 (Mph. 30)
Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Genesis 6-10 (Mph. 10)
Na. 1: Genesis 9:18-29 mpaka 10:1-7 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: Mmene Mungayankhire Ngati Wina Wanena Kuti, ‘Ngati Umakhulupirira Yesu, Palibe Vuto Ndi Tchalitchi Chimene Umakapempherako’—rs tsa. 93 ndime 2 (Mph. 5)
Na. 3: Kodi Mkhristu Angathetse Bwanji Chizolowezi Choseweretsa Maliseche?—lv tsa. 218-219 (Mph. 5)
Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 10: Kufunika Kobwereza Mfundo Zazikulu Tikakhala mu Utumiki. Nkhani yochokera m’buku la Sukulu ya Utumiki, tsamba 206 ndi 207. Chitani chitsanzo chachidule chosonyeza mfundo imodzi yomwe tikuphunzira m’nkhaniyi.
Mph. 10: Amuna Otumikira Bwino. (1 Tim. 3:13) Funsani atumiki othandiza awiri. Kodi ntchito yawo mu mpingo ndi yotani, ndipo amaichita bwanji? N’chifukwa chiyani anayesetsa kuti ayenerere kukhala atumiki othandiza? N’chifukwa chiyani amasangalala ndi kutumikira mu mpingo komanso kuthandiza akulu?
Mph. 10: “Tengerani Chitsanzo kwa Aneneri—Mika.” Mafunso ndi mayankho.
Nyimbo Na. 35 ndi Pemphero