Ndandanda ya Mlungu wa December 9
MLUNGU WOYAMBIRA DECEMBER 9
Nyimbo Na. 29 ndi Pemphero
□ Phunziro la Baibulo la Mpingo:
jr mutu 4 ndime 15-20 (Mph. 30)
□ Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: 1 Yohane 1-5; 2 Yohane 1-13; 3 Yohane 1-14 mpaka Yuda (Mph. 10)
Na. 1: 1 Yohane 5:1-21 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: Kodi Tiyenera Kumukumbukira Bwanji Yesu Khristu?—Luka 1:32, 33; Yoh. 17:3 (Mph. 5)
Na. 3: Chipembedzo Choona Chimachita Zinthu Zosonyeza Kuti Chimakhulupirira Yesu Khristu—rs tsa. 89 ndime 5 (Mph. 5)
□ Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 15: Sukulu ya Utumiki wa Mulungu ya 2014. Nkhani yokambidwa ndi woyang’anira sukulu. Pogwiritsa ntchito malangizo amene ali mu ndandanda ya Sukulu ya Utumiki wa Mulungu ya 2014, kambiranani mfundo zimene mukuona kuti n’zofunika kwambiri mu mpingo wanu. Komanso, ngati nkhani Na. 2 ndi Na. 3 zachokera m’buku la Kukambitsirana, onetsetsani kuti mukukonzekera ndime zokhazo zimene chiganizo chake choyambirira chayambira mkati pang’ono. Limbikitsani onse kuti azikonzekera mwakhama nkhani zawo, azipereka ndemanga pa mfundo zazikulu za Baibulo, komanso azigwiritsa ntchito malangizo ochokera m’buku la Sukulu ya Utumiki amene amaperekedwa mlungu uliwonse.
Mph. 15: “Kodi Tingakonzekere Bwanji Mawu Oyamba Okopa Chidwi?” Mafunso ndi mayankho. Chitani zitsanzo ziwiri zogawira buku la Baibulo Limaphunzitsa Chiyani. Chitsanzo choyamba chikhale chosagwira mtima, pamene chachiwiri chikhale ndi mawu oyamba okopa chidwi.
Nyimbo Na. 60 ndi Pemphero