Ndandanda ya Mlungu wa April 8
MLUNGU WOYAMBIRA APRIL 8
Nyimbo Na. 123 ndi Pemphero
□ Phunziro la Baibulo la Mpingo:
bt mutu 21 ndime 8-13 ndi bokosi patsamba 169 (Mph. 30)
□ Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Luka 10-12 (Mph. 10)
Na. 1: Luka 12:1-21 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: N’chifukwa Chiyani Anthu a Mtundu Wina Amakhala Osiyana Ndi a Mtundu Wina?—rs tsa. 235 ndime 5-tsa. 237 ndime 1 (Mph. 5)
Na. 3: N’chifukwa Chiyani Timaona Kuti Yehova Ndi Atate Wathu?—Mat. 6:9 (Mph. 5)
□ Msonkhano wa Utumiki:
Mph 10: Mungathe Kulimbikitsa Ena. (Aroma 1:11, 12) Nkhani yokambirana ndipo ikambidwe ndi woyang’anira utumiki. Tchulani chiwerengero cha apainiya okhazikika mu mpingo wanu. Tchulani mmene tingawalimbikitsire, monga kuwayamikira, kuyenda nawo mu utumiki, kuwapatsako ndalama zoyendera kapena kuwaitanira chakudya. Pemphani apainiya okhazikika kuti afotokoze mmene ena awalimbikitsira. Ngati mu mpingo wanu mulibe apainiya okhazikika, kambiranani mmene tingalimbikitsire anthu amene akuchita upainiya wothandiza.
Mph 10: Kuyankha Mafunso Okhudza Masiku Otsiriza. Nkhani yokambirana ndi omvera yochokera m’buku la Kukambitsirana, tsamba 268, ndime 6, mpaka tsamba 270, ndime 2. Chitani chitsanzo chosonyeza mmene mungagwiritsire ntchito mfundo imodzi ya m’nkhaniyi.
Mph 10: “Tengerani Chitsanzo kwa Aneneri—Yona.” Mafunso ndi mayankho.
Nyimbo Na. 13 ndi Pemphero