Ndandanda ya Mlungu wa January 12
MLUNGU WOYAMBIRA JANUARY 12
□ Phunziro la Baibulo la Mpingo:
cl-CN mutu 12, ndime 12-21 ndi bokosi
□ Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Genesis 6-10
Na. 1: Genesis 9:1-17
Na. 2: Kuyankha Anthu Amene Amanena Kuti Sakhulupirira Mulungu (rs-CN tsa. 311 ndime 4 mpaka tsa. 312 ndime 2)
Na. 3: Kalata Yochokera kwa Mulungu Amene Amatikonda (lr-CN mutu 2)
□ Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 5: Zilengezo za pampingo.
Mph. 10: Phindu Lokhala ndi Maganizo Abwino Muutumiki. Kukambirana ndi omvera. Yesu ankaona kuti anthu amene ankawalalikira anali ngati nkhosa zofunika kuthandizidwa ndipo chimenechi ndi chitsanzo chabwino kwa ife. (Mat. 9:36-38) Hananiya atauzidwa kuti akakumane ndi Saulo, anakayikira koma kenako anasintha. Kodi n’chiyani chinamuthandiza kusintha maganizo? (Mac. 9:13-15) Kodi zimene ananena atafika kwa Saulo zikusonyeza bwanji kuti Hananiya anali ndi maganizo abwino? (Mac. 9:17) Kodi n’chifukwa chiyani tiyenera kukhala ndi maganizo abwino tikamakambirana ndi anthu a m’gawo lathu? Kodi kukhala ndi maganizo abwino kungathandize bwanji kuti utumiki wathu ukhale wobala zipatso? Funsani wofalitsa mmodzi kapena awiri kuti afotokoze mwachidule mmene kukhala ndi maganizo abwino kunathandizira kuti utumiki wawo ukhale ndi zotsatira zabwino.
Mph. 10: Kodi Buku la Kukambitsirana za m’Malemba Tingaligwiritse Ntchito Bwanji? Nkhani yokambidwa ndi woyang’anira utumiki kapena mkulu wina aliyense, yochokera m’buku la Kukambitsirana, tsamba 7 ndi 8.
Mph. 10: “Adzamva Bwanji?”a
[Mawu a M’munsi]
a Mawu anu oyamba asafike mphindi imodzi, ndiyeno kambiranani mwa mafunso ndi mayankho.