Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w99 12/15 tsamba 9-13
  • Kupeza Mtendere Weniweni M’dziko Lamavuto

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kupeza Mtendere Weniweni M’dziko Lamavuto
  • Nsanja ya Olonda—1999
  • Timitu
  • “Ndikadzakula, Ndidzakhala wa IRA!”
  • Kusaloŵerera M’zandale N’koteteza Zedi
  • “Chonditchinjiriza Chinali Mfuti Zanga Zokha Basi”
  • “Zinthu Zinali Zopanda Tanthauzo Lililonse”
  • “Nthaŵi Zonse Mbonizo Zinkatilozera ku Baibulo”
Nsanja ya Olonda—1999
w99 12/15 tsamba 9-13

Kupeza Mtendere Weniweni M’dziko Lamavuto

“Chilombo chochititsa mantha cha ziwawa za magulu ampatuko chatulukira kunja tsopano,” linatero lipoti lina kalero mu 1969. Inali nthaŵi pomwe Mavuto, nyengo yamakono ya zipolowe ku Northern Ireland, anayamba kuwonjezereka.

IWAWA limodzi ndi kuphana zoyambitsidwa ndi magulu ampatuko zinafalikira ponseponse pomwe Apulotesitanti ndi Akatolika akuphawo, “amuna auchinyama kumbali zonse ziŵiri” zosagwirizana pazandale ndi m’chipembedzo, analimbika kumenya nkhondo yolimbirana ulamuliro mu Ireland. Chiyambire nthaŵi imeneyo “anthu oposa 3,600 aphedwa ndipo enanso zikwizikwi alemalitsidwa pa ziwawa zomwe zakhala zikuchitika kwa zaka pafupifupi 30,” inatero magazini yotchedwa The Irish Times.

N’zoona kuti nkhondo imeneyi n’njakalekale. Yakhala ikuchitika m’Ireland kwa mazana ambiri azaka. M’zaka zaposachedwapa, nkhondo imeneyi yawonongetsa zinthu zambiri ku Northern Ireland, koma miyoyo ya anthu m’Ireland yense yasautsidwa ndi zoŵaŵa ndi kusagwirizana zomwe nkhondoyo yadzetsa.

M’zochitika monga zimenezi, kwa zaka zoposa zana limodzi tsopano, Mboni za Yehova zakhala zikunena za njira yeniyeni yothetsera mavuto omwe akantha dziko lamavuto lino. Njira yothetsera mavuto imeneyo ndiyo Ufumu wa Mulungu m’manja mwa Yesu Kristu. (Mateyu 6:9, 10) Pomwe Mavutowo amayamba kumene mu 1969, ku Ireland kunali Mboni za Yehova zokwana 876. Tsopano kuli zopitirira pa 4,500, mu mipingo yoposa 100. Pano pali zomwe zinachitikira ena omwe afulatira zochita zandale ndi zankhondo.

“Ndikadzakula, Ndidzakhala wa IRA!”

Michaela anakulira m’chipembedzo cha Katolika m’dziko la Republic of Ireland. Kusukulu anaphunzira chinachake chokhudza mbiri ya Ireland ndi kusagwirizana kwake ndi dziko la Britain komwe kwatha mazana ambiri azaka. Monga mwana, anayamba kudana kwambiri ndi Angelezi, omwe ankawaona ngati “opondereza anthu a ku Ireland.” Ali ndi zaka khumi, anauza agogo ake aakazi kuti, “Ndikadzakula, ndidzakhala wa IRA!” (The Irish Republican Army) “Anandiwomba khofi kumaso lomwe mpakana lero ndimalikumbukirabe,” Iye akusimba motero. Anadziŵa mochedwa kuti agogo ake aamuna anali msilikali wa gulu lankhondo la ku Britain m’nkhondo yoyamba yapadziko lonse. Panthaŵi inayake agogo ake aakazi anaimira agogo ake aamunawo kutsogolo kuwateteza kuti asilikali a IRA asawawombere.

Komabe, Michael atakula anali wofunitsitsa kuchitapo chinachake kuti ateteze Akatolika anzake ku Northern Ireland. “Ine panthaŵiyo,” iye akutero, “ndinkaona ngati kuti anthu okhawo omwe amachita chilichonse kuthandiza Akatolika ku Northern Ireland anali a IRA.” Posonkhezeredwa ndi zomwe anazilingalira kukhala zifukwa zabwino, anakhala membala wagulu la IRA ndipo anaphunzitsidwa mmene angagwiritsire ntchito zida. Anzake ena atatu anaphedwa ndi asilikali achipulotesitanti ku Northern Ireland.

Pambuyo pake Michael anataya mtima ndi nkhondo za magulu a asilikaliwo, mwachitsanzo, anasokonezeka ndi udani waukulu womwe unali m’magulu osiyanasiyana a asilikaliwo. Ataikidwa m’ndende atalakwa pa zinthu zina zokhudzana ndi zochita za IRA, anapemphera kwa Mulungu kuti amuthandize kupeza njira yeniyeni yomka nayo ku mtendere wosatha ndi chilungamo. Patapita nthaŵi Mboni za Yehova zinafika panyumba pake. Komabe, udani wakale unaika chotchinga. Mbonizo zinali zachingelezi. Chidani chake chokhazikika kwambiricho chinapangitsa kuti kukhale kovuta kwa iye kumvetsera. “Nthaŵi zonse sindinkasonyeza kuti ndikusangalala ndi kubwera kwawo,” iye akutero, “koma anachitabe khama kumabwera ndi kumadzalankhula nane, ndipo ndinayamba kuona kuti Ufumu wa Mulungu ungathetse kusoŵa chilungamo kwa andale ndi anthu wamba komwe ine ndinkalimbana nako kuti ndikuthetse.”​—Salmo 37:10, 11; 72:12-14.

Nthaŵi yovuta inafika tsiku lina madzulo pamene Michael anakumana ndi mkulu wa gulu lake wa IRA, yemwe anati, “Tili ndi ntchito yoti iwe ugwire.” “Ndinalingalira kuti kunali koyenera kusankha chochita nthaŵi yomweyo,” akutero Michael, “choncho ndinapuma ndi mphamvu ndiyeno n’kunena kuti, ‘tsopano ndine wa Mboni za Yehova,’ ngakhale kuti panthaŵiyo ndinali wosabatizidwa. Ndinadziŵa ndithu kuti ndikufuna kukhala mtumiki wa Yehova.” Koma wolamulira wamkuluyo anayankha kuti: “Tidzakuimika pakhoma ndikukuwombera.” Mosasamala kanthu za kuopsezedwa kumeneku, Michael analisiya gulu la IRA. Analimba mtima kuti achite zimenezi mwa kulola Mawu a Yehova kukhudza maganizo ndi mtima wake. “Patapita nthaŵi, mkazi wanga ndi ana anga ena anapatuliranso miyoyo yawo kwa Yehova. Tili ndi mtendere weniweni tsopano m’mitima yathu. Ndipotu nthaŵi zonse tizithokoza Yehova polola kuti tiphunzire choonadi ndi kufalitsa nawo uthenga wamtendere m’dziko lamavuto.”​—Salmo 34:14; 119:165.

Kusaloŵerera M’zandale N’koteteza Zedi

“Ndinakulira kumudzi m’chigawo cha County Derry m’dziko la Northern Ireland,” akutero Patrick. “Monga mwana, palibe china chilichonse chomwe ndinkadziŵa koma Mavuto basi. Mkhalidwe umenewo unakhudzadi kaonedwe kanga ka zinthu ndiponso malingaliro anga.” Patrick anatengeka maganizo kwambiri ndi ziwembu za utundu ndi tsankhu lodana ndi anthu a ku Britain. Iye anaona anthu azipembedzo kumbali zonse za magulu olimbana m’zandale akuswa mfundo zachikhalidwe zikuluzikulu zachikristu komanso mfundo zina zikuluzikulu za makhalidwe abwino a anthu. Zotsatira zake zinali zakuti, anasiya chipembedzo, pang’ono ndi pang’ono anadzakhala wokhulupirira kuti kulibe Mulungu ndiponso anazama kwambiri m’zikhulupiriro zopanda maziko za Karl Marx.​—Yerekezani ndi Mateyu 15:7-9; 23:27, 28.

“Ndimakumbukirabe zomwe zinachitika kalelo, Kumpoto, akaidi odana ndi ulamuliro wa Britain ananyanyala chakudya,” akutero Patrick. “Zinandikhudza kwambiri. Ndikukumbukira kuti ndinkakweza mbendera za Ireland ndi kulemba mawu onyoza Abulitishi m’zipupa ndi pena paliponse pomwe ndikanatha kutero. Ndili ndi zaka 15 zokha, ndinali kalinde pamaliro a mmodzi wa onyanyala chakudya aja yemwe anafera m’ndende.” Monganso ena ambiri omwe analoŵerera m’zipwirikiti ndi chisokonezo m’nthaŵiyo, Patrick anachita nawo zipolowe ndi zionetsero zomwe ankaziona ngati chilungamo cha anthu ndi ufulu wolingana. Anayamba maubwenzi ndi omenyera ufulu ambiri omwe ambiri a iwo anaikidwa m’ndende ndi akuluakulu a boma la Britain.

“Kenako” akutero Patrick, “chifukwa cha nkhani ya zachuma, mapeto ake ndinapezeka ndili ku England. Ndidakali komweko, apolisi a boma la Britain anamanga mnzanga wina yemwe ankakonza zophulitsa mabomba.” Ngakhale kuti Patrick ankagwirizanabe kwambiri ndi zochita za omenyera ufuluwo, maganizo ake anayamba kusintha. Anayamba kuona kuti kudana kwake ndi Angelezi onse kunali kopanda maziko enieni. “Ndinayambanso kuzindikira,” iye akutero, “kuti zochita za magulu a asilikali amenewo sizingathetse mavuto ndi kuchotsa kupanda chilungamo komwe kunkandisoŵetsa mtendereko. Kunali katangale wadzaoneni ndi kupanda chilungamo kosiyanasiyana pakati pa omwe ankalamulira magulu a asilikali amenewo.”​—Mlaliki 4:1; Yeremiya 10:23.

Pambuyo pake Patrick anabwerera ku Northern Ireland. “Nditabwerera, mnzanga anandisonyeza kwa Mboni za Yehova.” Kupyolera m’kuphunzira kwake Baibulo ndi Mboni, Patrick anayamba kuona njira yeniyeni yothetsera nkhondo za anthu ndi kusagwirizana. Anapita patsogolo mwauzimu mofulumira kwambiri pamene mfundo zachikhalidwe za m’Baibulo zinakhudza maganizo ndi mtima wake. (Aefeso 4:20-24) Iye anati: “Tsopano, m’malo molinganiza zothetsa dongosolo la zandale ndi mikhalidwe ya anthu yomwe ilipo, ndinayamba kulalikira uthenga wa mtendere wochokera m’Baibulo, ngakhale m’madera momwe munali anthu okonda ulamuliro wa Britain momwe poyambirira sindikanayerekeza n’komwe kukaonekera m’dera limenelo. Ndithudi, panthaŵi yomwe kuphana kwa magulu ampatuko mu Belfast kunali kosaneneka, anthu okhawo omwe anali kuyenda momasuka pakati pa dera la anthu okonda ulamuliro wa Britain ndi dera la odana ndi ulamulirowo popanda magalimoto ankhondo zinali Mboni za Yehova.” Monganso Mboni zina ku Northern Ireland panthaŵi imeneyi, iye anaona kuti kusaloŵerera m’ndale, monga momwe Akristu oyambirira ankachitira, kulidi chotetezera chenicheni. (Yohane 17:16; 18:36) Anamaliza ndi mawu akuti: “N’komasula zedi kuona kuti Yehova kupyolera mwa Yesu Kristu adzapereka chilungamo chenicheni ndi ufulu kuchotsa kuponderezana kwa mtundu wonse wa anthu.”​—Yesaya 32:1, 16-18.

“Chonditchinjiriza Chinali Mfuti Zanga Zokha Basi”

“Ndinakulira kumbali ina ya kugaŵanika kwa ndale ndi chipembedzo,” akutero William. “Ndinali wozama zedi m’tsankhu losaneneka la Chipulotesitanti ndipo ndinkadana kwambiri ndi china chilichonse cha Chikatolika. Sindinkaloŵa ngakhale m’sitolo ya Mkatolika ngati kunali kotheka kutero, ndipo ku Republic of Ireland ndinapitako kamodzi kokha basi. Ndinaloŵa m’magulu ndi mabungwe osiyanasiyana a Chipulotesitanti monga la Orange Order, gulu lomwe n’lodzipereka kuteteza Chipulotesitanti ndi chikhalidwe chawo.” Ali ndi zaka 22, William analoŵa m’gulu la Ulster Defense Regiment, mbali ya gulu lankhondo la Abulitishi lomwe limalemba ntchito anthu akomweko. Ambiri a mamembala ake anali Apulotesitanti. Anali okonzekera kupha kuti ateteze chikhalidwe chake. “Ndinali ndi mfuti zambiri ndipo ndinali wotsimikizira kuzigwiritsa ntchito ngati panafunikira. Imodzi ndinkaiika pansi pa mtsamiro wanga usiku.”

Ndiyeno kenako posinthira zinthu panafika. “Ndinayamba kuzindikira kuti Mboni za Yehova zili ndi chinachake chapadera pamene ndinkagwira ntchito yokonzanso nyumba inayake yakalekale ndi mmodzi wa iwo. Wantchito mnzanga ameneyu anandikopa maganizo kwambiri. Tikumangira limodzi nyumbayo, ndinali wokhoza kum’funsa mafunso ambiri omwe ankandisoŵetsa mtendere okhudza Mavuto, chipembedzo, ndi Mulungu. Mayankho ake apafupi ndi omvekawo anandithandiza kufikira pa kuzidziŵa bwino zedi Mboni za Yehova​—gulu la anthu ogwirizana, osachita ziwawa ndi osaloŵerera m’zandale, odziŵika chifukwa cha kukonda kwawo Mulungu ndi anansi awo.”​—Yohane 13:34, 35.

Patangopita miyezi inayi yokha chiyambire kuphunzira Baibulo, William anachoka m’magulu achipembedzo ndi andale momwe iye anali. Iye akukumbukira kuti: “Kumeneku kunali kusintha kwakukulu kwa ine, chifukwa ndinafunikira kusiya miyambo yambiri yapamtima yomwe ndinakhala ndikuchita kwanthaŵi yaitali.” Komabe, chiyeso chake chachikulu chinali chisanadzebe. “Chifukwa cha momwe zinthu zinalili ku Northern Ireland, ndinaona kuti panalibe choti chinganditchinjirize choposa mfuti zangazo. Gulu la asilikali la IRA linkandiona kukhala ‘woyenera kufa.’ Choncho kunali kovuta kwambiri kuleka kugwiritsa ntchito zida zimenezi.” Komabe, pang’ono ndi pang’ono uphungu wa m’Baibulo, monga womwe ukupezeka pa Yesaya 2:2-4, unasintha malingaliro ake. Pambuyo pake anaona kuti Yehova ndiye anali mtetezi wake weniweni, monga momwedi analili kwa Akristu m’zaka zana loyamba. Kenako William anachotsa mfuti zakezo.

William akuti: “Chimodzi mwa zinthu zomwe ndikusangalala nazo kwambiri n’chakuti tsopano ndili ndi ubwenzi wakuya ndi wosatha ndi anthu omwe likanakhala kale lija ndikanawaona ngati adani oipitsitsa. Ndiponso, kukhala wokhoza kutengera uthenga wa m’Baibulo wa chiyembekezo ku madera omwe kale anali oletsedwa kwa ine kulidi magwero enieni a chimwemwe. Kulingalira zomwe choonadi chachita kwa ine ndi banja langa kumandipangitsa kukhala woyamikira Yehova ndi gulu lake kosatha.”

“Zinthu Zinali Zopanda Tanthauzo Lililonse”

Robert ndi Teresa anachokera m’mabanja amikhalidwe yosiyana kwambiri. “Ine ndikuchokera m’banja lokhulupirika kwambiri m’chipembedzo cha Chipulotesitanti,” akutero Robert. “Abale anga ena aloŵetsedwa m’zochita za magulu a asilikali apadera. Ndipo ine ndinaloŵa m’gulu lankhondo lachibulitishi la Ulster Defense Regiment ndili ndi zaka 19. Ndinkathera nthaŵi yambiri ndikulondera dera lomwe Teresa ankakhala. Usiku wina anandipatsa ntchito zina m’malo mwa ntchito yanga yamasiku onse yolonderayo. Usiku umenewo galimoto ya Land-Rover yomwe ine ndikanakhala ndikuyendera inaphulitsidwa. Asilikali aŵiri anafa ndipo enanso aŵiri anavulala.”

Robert anayamba kulingalira za tanthauzo la moyo. “Nthaŵi zonse ndinkakhulupirira Mulungu, koma n’tayang’anayang’ana mu Northern Ireland, zinthu zinali zopanda tanthauzo lina lililonse kwa ine. Mosazengereza ndinayamba kupemphera kwa Mulungu. Ndinafunsa Mulungu ngati iye analikodi, ndipo ngati aliko, ndinam’pempha kuti andionetse njira yabwino yokhalira ndi moyo. Ndikukumbukira ndikumuuza Mulungu kuti kuyenera kuti kwina kwake kuli chipembedzo chimodzi choona!” Masiku owerengeka pambuyo pake, wa Mboni za Yehova anafikira Robert ndipo anam’siyira mabuku ena. Atabwera kunyumba kuchokera kumalo omwe amayendera usiku umenewo, Robert anayamba kuwaŵerenga ndikuwamaliza faifi koloko m’maŵa. “Mwamsanga ndinazindikira choonadi,” iye akutero, “ndipo ndinali wokhoza kuona kuti chilichonse chikuchokera m’Baibulo.” (2 Timoteo 3:16) Anayamba kuphunzira Baibulo, ndipo mosakhalitsa, anapatulira moyo wake kwa Mulungu.

“Nthaŵi Zonse Mbonizo Zinkatilozera ku Baibulo”

Kumbali ina, Teresa, anachokera m’banja la Katolika, lodana koopsa ndi ulamuliro wa Britain. “Monga msungwana, ndinaloŵa chipani cha Sinn Féin.”b Teresa akuvomereza kuti: “Zimenezi zinandipangitsa kuti ndiyambe kumathandiza m’zochitika za magulu a asilikali. Ndinkathandiza kupeza ndalama zothandizira pankhondo. Ndinkadziŵitsa gulu la IRA za zomwe zinali kuchitika m’dera langa. Ndinalinso kuchita nawo zipolowe ndi kuponyera miyala apolisi ndi asilikali olondera malo.”

Ena a m’banja la Teresa atayamba kuphunzira Baibulo ndi Mboni za Yehova, chidwi chake nayenso chinakula. Mphamvu ya Mawu a Mulungu inam’sonkhezera kwambiri. “Mbonizo zinkatilozera ku Baibulo nthaŵi zonse kuti tipezemo mayankho a mafunso,” Iye akutero. “Lonjezo lomwe lili pa Danieli 2:44 linalidi lotsegula maso. Ndinaona kuti Ufumu wa Mulungu unalidi njira yeniyeni yochotsera kupanda chilungamo konse komwe ine ndinkalimbana nako.” Kunyansidwa ndi nkhanza zina zochitidwa ndi magulu a asilikali kunayamba kukula mwa iye. Mwachitsanzo, Teresa sankamvetsa chifukwa chake aliyense wachifundo ndi wa mikhalidwe yaumunthu angakhalire wosangalala pakumva nkhani ya uchigaŵenga yoti asilikali ngakhale anthu wamba aphedwa kapena kulumalitsidwa ndipo mabanja awo ali pachisoni chachikulu ndi nkhaŵanso yaikulu. Teresa nayenso anachita chidwi ndi choonadi cha m’Baibulo ndi kulola mfundo za chikhalidwe za Mulungu kusintha kaganizidwe kake. Anapatulira moyo wake kwa Mulungu ndipo posakhalitsa anabatizidwa.​—Miyambo 2:1-5, 10-14.

Teresa anakumana ndi Robert pamene onseŵa amasonkhana nawo pa mpingo wina wa Mboni za Yehova ku Northern Ireland. Iye akuthirira ndemanga kuti: “Nditakumana ndi Robert kwanthaŵi yoyamba, zinandivuta kwambiri kukhulupirira kuti ndinalidi kulankhula modekha komanso mwamtendere ndi munthu yemwe, kufikira posachedwa pompa, n’kanamuganizira kukhala womenyera nkhondo kumbali ya Abulitishi. Ndithudi Mawu a Mulungu anandithandiza kuchotsa chidani ndi tsankhu zomwe zinali zitakhazikika mwa ine.” Iye ndi Robert aona kuti mmalo mogaŵanika chifukwa cha udani ndi tsankhu zodzetsedwa ndi kusiyana kwawo miyambo ndi chikhalidwe, tsopano adali ndi zinthu zambiri zofanana. Champhamvu kwambiri mwa zinthu zimenezi chinali kukonda Yehova Mulungu. Anakwatirana. Tsopano amagwirira limodzi ntchito yopereka uthenga wa Mulungu wa mtendere weniweni kwa anthu amikhalidwe ndi zikhulupiriro zosiyanasiyana m’dziko lamavuto limeneli.

Enanso ku Ireland akumana ndi zinthu zofananazi. Mwa kumvetsera ndi kulandira chiphunzitso cha Mawu ouziridwa a Mulungu, athaŵa ‘nzeru ndi chinyengo chopanda pake’ cha anthu. (Akolose 2:8) Tsopano aika chidaliro chawo chonse m’malonjezo a Mulungu olembedwa m’Baibulo. Ali okondwa kugaŵana ndi wina aliyense yemwe akamvetsera chiyembekezo chawo cha m’tsogolo mwamtendere, momwe simudzakhalanso ziwawa zochititsidwa ndi magulu ampatuko kapena za mtundu wina uliwonse.​—Yesaya 11:6-9.

[Mawu a M’munsi]

a Mayina asinthidwa.

b Chipani chandale chogwirizana kwambiri ndi gulu lankhondo la Provisional IRA.

[Zithunzi patsamba 10]

Nkhondo ya pakati pa magulu a asilikaliyo aijambula moitamanda m’zipupa mu Northern Ireland monse

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena