Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w94 9/15 tsamba 8-9
  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Nigeria

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Nigeria
  • Nsanja ya Olonda—1994
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Achichepere Akalimira Upainiya
  • Vidiyo ndi Nyumba Yaufumu
  • Mboni Za Yehova—Gulu la Dzinalo
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Apainiya Amapereka ndi Kulandira Madalitso
    Nsanja ya Olonda—1994
Nsanja ya Olonda—1994
w94 9/15 tsamba 8-9

Mboni za Yehova Padziko Lonse​—Nigeria

NIGERIA ali ngati wosomekedwa pangodya ya mmunsi mwa chitunda chakumadzulo cha Afirika. Wokhala pa Gulf of Guinea, iye ali kumpoto pang’ono kwa equator ndipo ali ndi nzika zoposa 88 miliyoni.a

Mkati mwa zaka zautumiki ziŵiri zapitazo, ofesi ya nthambi ya Watch Tower Society ya Nigeria yapereka chisamaliro chapadera kwa achichepere. Kufufuza kwa m’mipingo ya Mboni za Yehova kunasonyeza kuti 80 peresenti ya awo omwe anayamba kulalikira mbiri yabwino mu Nigeria mkati mwa 1992 anali pakati pa misinkhu ya zaka 10 ndi 20. Pa awo obatizidwa mkati mwa chakacho, 63 peresenti anali a msinkhu wa gulu limenelo.

Achichepere Akalimira Upainiya

Achichepere ambiri akuloŵa ntchito yolalikira yanthaŵi yonse monga apainiya. Mpainiya wina wotchedwa Hannah akuti: “Pamene ndinali pafupi kumaliza sukulu, ndinakachezera amene anali pa Sukulu Yautumiki Waupainiya, kumene ndinakumana ndi alongo okalamba aŵiri. Ndinalingalira kuti, ‘Ngati aŵiri aja angachite upainiya, nchifukwa ninji sindingatero?’

“Motero nditamaliza sukulu, ndinakhala mpainiya. Pambuyo pa miyezi itatu ndinakumana ndi Josephine wa zaka zakubadwa 26, wolambira matsenga. Iye anati: ‘Inu Mboni za Yehova ndinu anthu oipa. Simumakondwerera Krisimasi kapena kugwiritsira ntchito njirisi.’ Ndinayankha kuti ngati akandilola kuphunzira naye Baibulo, akadziŵa chifukwa chake sitimachita zinthu zimenezo. Iye anandipempha kupitanso. Posapita nthaŵi anayamba kufika pamisonkhano ndipo anapanga masinthidwe ambiri m’moyo wake. Mu December 1990 anabatizidwa. Chiyambire August 1991, Josephine wakhala mpainiya. Pamene analoŵa Sukulu Yautumiki Waupainiya chaka chatha, anandidziŵikitsa kwa a m’kalasi anzake monga amayi wake wauzimu!”

Vidiyo ndi Nyumba Yaufumu

Imodzi ya mavidiyo ojambulidwa a Sosaite inathandiza mpingo waung’ono kugula malo a Nyumba ya Ufumu. Pofunafuna kogula malo, abale anayi anafikira Onojie, nyakwaŵa wa dera limenelo. Iye anawapatsa puloti pa 20,000 naira ($1,025, U.S.). Mpingowo sukanatha kulipira ndalama zimenezo, popeza kuti panali ofalitsa 17 okha olipirira ntchitoyo. Onojie ameneyo ananena kuti akalingalira za malo ena.

Pambuyo pa miyezi ingapo, mmodzi wa akulu a mpingowo anakacheza kunyumba kwa Onojie. Onojie anali kuonerera vidiyo ya kulongedwa unyakwaŵa kwake. Mkuluyo anati: “Ndili ndi vidiyo imene ndingakonde kuti muione. Imatchedwa kuti Jehovah’s Witnesses​—The Organization Behind the Name.”

Pambuyo pake, mkuluyo anafunsa zimene Onojieyo analingalira ponena za vidiyoyo. “Ndinaonerera kanemayo kasanu konse,” anatero Onojie. Mkuluyo anakumbutsa Onojie za Nyumba Zaufumu zimene anaona m’vidiyo ndi kulongosola kuti mpingo wakumaloko unafuna kumanga yofanana ndi zimenezo. Ndiyeno mkuluyo anafunsa ngati mpingo ukanagula malo oyandikana ndi puloti yake yaing’ono. Onojie anayankha kuti: “Usiku wapitawu nditatha kuonerera vidiyo ija, ndinalingalira chinthu chimodzimodzicho.” Atatero, anapima mamita asanu ndi imodzi a malo oyandikana ndi malo a mpingo. “Mungatenge ameneŵa,” iye anatero. “M’litali mungatenge monga momwe mufunira. Konzetsani zikalata, ndipo ndidzazisaina.”

[Mawu a M’munsi]

a Kuti mudziŵe zowonjezereka, onani Kalenda ya Mboni za Yehova ya 1994.

[Bokosi patsamba 9]

ZIŴERENGERO ZA DZIKOLO

Chaka Chautumiki cha 1993

CHIŴERENGERO CHAPAMWAMBA CHA OCHITIRA UMBONI: 174,582

KUGAŴA: Mboni 1 pa anthu 507

OFIKA PACHIKUMBUTSO: 473,245

AVAREJI YA OFALITSA AUPAINIYA: 19,777

AVAREJI YA MAPHUNZIRO A BAIBULO: 242,028

CHIŴERENGERO CHA OBATIZIDWA: 8,888

CHIŴERENGERO CHA MIPINGO: 3,289

OFESI YA NTHAMBI: BENIN CITY, BOMA LA EDO

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena