Kuchita ndi Zofooka Zanga
Monga yasimbidwa ndi Thomas Addison
PAMENE ndinali mnyamata wamng’ono, kungowona mbalame yosawopsya iri panjira ndinkathaŵa kukalambalala kutali. Pamene achibale kapena mabwenzi anabwera kudzacheza, iwo ankapeza mwana wosalankhuzika ali kumbuyo kwa siketi ya amayi ake. Nthaŵi zonse kutabwera alendo ndinkanthaŵira mwa mwamsanga monga mmene ndikanathera ku chipinda chogona. Lilime langa linamangika pamene ndinali pamaso pa aliyense wokhala mu ulamuliro, makamaka aphunzitsi apasukulu.
Kodi nchiyani chimene chinanditheketsa kusintha? Kodi ndimotani mmene wachichepere wamanyazi oipa moterowo anakhalira wokhoza kulankhula zaka zaposachedwapa ku magulu a zikwizikwi za anthu pa misonkhano yaikulu?
‘Kuwongola’ kwa Makolo
Makolo anga—makamaka Atate, mwamuna wa ku Scotland wowonda, wamphamvu—anandipeza kukhala mwana wovuta kumvetsetsa. Pokhala amasiye pa msinkhu wa zaka 13 zakubadwa, iwo anawonekadi amwano komabe achibadwa chabwino. Anadziŵa kudzisunga okha kuyambira pa msinkhu wachichepere. Amayi, kumbali ina, anali mwana wa mlimi ndipo anali aumunthu wodekha. Kuphunzitsidwa kwanga kuyambira pa ubwana kunali kwabwino ndi kolimba, komabe kosachinjirizidwa mopambanitsa.
Pamsinkhu wa zaka zisanu ndi chimodzi, mu 1945, ndinawonekera kwa nthaŵi yoyamba pa Sukulu Yautumiki Wateokratiki. Nkhani yanga yoyamba ndinaiperekera mu nyali ya parafini mu mpingo waung’ono wa mabanja atatu okha mu Australia. Nthaŵi idakaliko, Atate anandithandiza kukonzekera, akumalongosola maubwino a kulankhula kwa mwadzidzidzi. Iwo anagogomezeranso kusachita mantha konse ndi zimene anthu anganene kapena kulingalira. Monga mmene ananenera: “Anthufe ndife miyulu ya fumbi. Miyulu ina njaikuluko kuposa ina, basi.” Mawondo anga ananthunthumira, zikhantho zinayamba kutulutsa thukuta, ndipo ndiri pakati pa nkhaniyo, ndinamangika lilime ndipo ndinalephera kumaliza.
Ndiyenera kukhala ndinali ndi zaka chifupifupi khumi pamene Atate anatitenga ine ndi mphwanga Robert kupita m’khwalala lalikulu la mzinda, kutsogolo kwanyumba yowonetsera kanema ya kumaloko. Kumeneko tinatukula magazine a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! m’maso mwa anzathu akusukulu. Magazinewo anamveka olemera ngati mtovu, ndipo nthaŵi zina ndinkawabisa kumbuyo! Ndinkayesayesa kuima m’malo osawonekera kwambiri.
Komabe, pamene ndinkapenya chitsanzo cha Atate cha kulimbika mtima, ndinalimbikitsidwa mokulira. Iwo nthaŵi zonse ananena kuti kuchita mantha kunali kugonjera kwa Satana ndi kuwopa anthu. Chiyeso china chinabwera pa sukulu. Nkhondo Yadziko ya II inali itangotha kumene, ndipo utundu mu Australia unali udakali wamphamvu. Mlongo wanga Ellerie ndi ine sitinkaimirira mkati mwa kusonkhana kwa sukulu pamene nyimbo yautundu inkaimbidwa. Ndinachipeza kukhala chiyeso chenicheni kuwonekera wosiyana, komanso chirikizo ndi chilimbikitso chanthaŵi zonse cha makolo anga zinandithandiza kusagonja.
Chitsanzo Chabwino cha Atate
Kulingalira kakulidwe ndi mkhalidwe wa Atate, iwo analidi oleza mtima ndi ine. Iwo anayamba kugwira ntchito pa migodi ya malasha mu England pamene anali mnyamata wa zaka 13 zokha. M’zaka zawo zoyambirira za m’ma 20, anasamukira ku Australia kukafuna moyo wabwinopo. Koma kutsika kwa zachuma kwa m’ma 1930 kunayamba, ndipo iwo analandira ntchito pansi pa mikhalidwe yovuta kwenikweni kuti asamalire banja lawo.
Atate anathedwa nzeru ndi mikhalidwe mwachisawawa ndipo makamaka ndi ndale zadziko, chotero pamene anaŵerenga mabukhu a Watch Tower Society ndi mmene ankavumbulira mopanda mantha chinyengo cha ndale zadziko, dongosolo la zamalonda, ndi chipembedzo, zinadzutsa chikondwerero mwa iwo. Pasanapite nthaŵi yaitali anadzipatulira kutumikira Yehova, mwamsanga pambuyo pakuti Amayi anatero. Mosasamala kanthu za kudwala m’mapapo kaamba ka kudirikiziridwa pa mgodi ndi kusakhala ndi luso lapadera la ntchito, Atate anatenga banja lathu kukatumikira m’malo kumene kunali kusoŵa kwauzimu. Chidaliro chawo pa Yehova chinasiya chitsanzo chozama pa ine.
Mwachitsanzo, ndikukumbukira pamene tinasamukira ku tauni yaing’ono ya mgodi wa malasha kumene Mboni zokha zokhalako zinali alongo aŵiri okalamba, onsewo anali ndi amuna osakhulupirira. Nyumba inali yovuta kupeza, koma pomalizira pake tinakhoza kuchita lendi nyumba yakale makilomita angapo kunja kwa tauni. Choyendera chathu chokha chinali pansi kapena panjinga. Kenaka, tsiku lina m’mamawa, pamene ana atatufe tinakakhala ndi mabwenzi kutali, nyumba inapsyeratu ndi moto. Makolo athu anathaŵa napulumutsa miyoyo yawo, koma palibe china chirichonse chimene chinapulumutsidwa. Tinalibe insuwalansi ndipo tinalibenso ndalama.
Atate ankakumbukira za zimenezi alipafupi ndi imfa yawo mu 1982. Iwo anati: “Kodi ukukumbukira, mwana wanga, mmene poyamba mkhalidwe unawonekera wakuda, koma Yehova anaima kumbali yathu? Nkulekeranji, pambuyo pa moto uja, abale a ku Perth anatumiza mipando, zovala, ndi ndalama. Chifukwa cha kuwoloŵa manja kwawo, tinakhala bwinopo kuposa poyambapo moto usanachitike!” Poyamba ndinalingalira kuti Atate anaganizira mopambanitsa pamene analankhula kwambiri za thandizo la Yehova m’miyoyo yathu. Komabe, zokumana nazo zobwerezabwereza za chimene anachitcha thandizo laumulungu zinachuluka kwambiri kosakhoza kuzilongosola m’njira ina iriyonse.
Kuganiza Kwabwino kwa Amayi
Limodzi la mavuto anga aakulu nthaŵi zonse lakhala kuganiza moipa. Amayi nthaŵi zonse ankandifunsa kuti: “Kodi nchifukwa ninji nthaŵi zonse umayang’ana ku mbali yoipa ya moyo?” Chitsanzo chawo cha kuyang’ana ku mbali yabwino chinali chisonkhezero kwa ine kumayesetsa kuganiza bwino.
Posachedwapa, Amayi anasimba za chochitika china m’tauni yaing’ono yaulimi mwamsanga titasamukirako. Ndemanga ya dokotala wakumaloko inawasangalatsa. Iye analingalira kuti makolo athu anali okhupuka, powona kavalidwe kawo kaudongo ndi mawonekedwe a kapesedwe kabwino. Chowonadi chinali chakuti nyumba yathu inali chimsasa chachikulu, chokhala ndi zipinda zogaŵidwa ndi masaka. Munalibe magetsi, gas, kapena madzi akumpopi. Tsiku lina ng’ombe inayesera kuthyola kuti iloŵe ku khomo la kutsogolo. Mungalote kumene ndinali: kunsi kwa bedi!
Amayi ankatunga madzi athu ku chitsime pa mtunda wa mamita chifupifupi 200, m’migomo iŵiri ya malita 15 umodzi yokoloŵekedwa ku goli lopingasa pamapeŵa pawo. Iwo anali ndi nzeru zakuwona mbali yoseketsa ya zovutitsa ndipo, ndi chisonkhezero china chochokera kwa Atate, anawona mkhalidwe wovuta uliwonse kukhala chitokoso chofunikira kugonjetsedwa mmalo mokhala chopinga. Iwo ankanena kuti ngakhale kuti tiribe zambiri zakuthupi, tinasangalala ndi madalitso abwino ambiri auzimu.
Mwachitsanzo, tinatha masiku ambiri achimwemwe kupita ku magawo akutali kukalalikira, kukhala pa msasa pansi pa nyenyezi, tikuphika nyama ya nkhumba ndi mazira pa moto wa nkhuni, ndi kumayimba nyimbo za Ufumu pamene tinkayenda. Atate ankaimba nyimbozo pa accordion yawo. Inde, m’njira zimenezi tinalidi olemera. M’matauni ena a kumidzi, tinachita lendi maholo aang’ono ndi kulengeza nkhani Zabaibulo, zimene tinkapereka pa Sande masana.
Nthaŵi zina, chifukwa cha kudwaladwala kwa Atate, Amayi anafunikira kugwira ntchito yakuthupi kuwathandizira kupeza ndalama. Kwa zaka zambiri iwo anasunga amayi awo ndi agogo aamuna ndipo pomalizira pake atate athu aŵiriwo asanamwalire. Iwo anachita zimenezi popanda kudandaula. Ngakhale kuti ndinachitabe tondovi kwa panthaŵi ndipo kaŵirikaŵiri ndinali ndi maganizo oipa, chitsanzo cha Amayi ndi kundikokosa kodekha kunandipatsa chikhumbo chakufuna kupitirizabe kuyesayesa.
Kuchita Ndi Tondovi
Kothera kwa zaka zanga zapakati pa 13 ndi 19, zofooka zanga zonse zakuubwana zimene ndinaganiza kuti zinatha zinabweranso mwamphamvu. Mafunso onena za moyo anadithetsa nzeru. Ndinayamba kuzizwa, ‘Kodi anthu onse ali ndi mwaŵi wolingana wa kumdziŵa ndi kumtumikira Yehova?’ Mwachitsanzo, bwanji ponena za mwana wobadwira mu India kapena China? Ndithudi mwaŵi wake wa kumdziŵa Yehova ukakhala wochepa kwenikweni kuposa ndi uja wa mwana wokhala ndi mwaŵi wa kuleredwa ndi makolo omwe ali Mboni. Izi zinawoneka kukhala kuchitira mosakomera! Ndiponso, zachibadwa zamajini ndi malo okhala, zimene mwana alibepo ulamuliro, ziyenera kuchita mbali yaikulu. M’njira zambiri, moyo unawoneka kukhala wopanda chilungamo. Ndinakangana ndi makolo anga kwa maola ambiri pa mafunso oterowo. Ndinadanso nkhaŵa ponena za mawonekedwe anga. Panali zinthu zambiri zimene sindinakonde ponena za ine mwini.
Pamene ndinasinkhasinkha pa nkhani zimenezi, zinandichititsa tondovi, nthaŵi zina kwa milungu yambiri. Ndinada mawonekedwe anga. Nthaŵi zambiri, ndinalingalira zakudzipha mwamseri. Panali nthaŵi zimene ndinkafuna kupeza chikhutiritso mwakumwerekera m’kudzimverera chisoni. Ndinadziwona kukhala ngati wofera chikhulupiriro womvetsedwa molakwa. Ndinapsyinjika ndipo pomwepo, mwadzidzidzi, ndinadzimva wochititsidwa mantha. Zonse zondizinga zinawoneka kusakhala zenizeni, ngati kuti ndinalikupenya pa zenera la nkhungu.
Chochitika chimenechi chinandipangitsa kuzindikira kuti kudzimverera chisoni nkwangozi kwenikweni. M’pemphero kwa Yehova, ndinalonjeza kupanga kuyesayesa kwamphamphu kusadzimvereranso chisoni. Ndinayamba kusumika maganizo pa malingaliro abwino, Amalemba. Kuyambira nthaŵi yomweyo kunkabe mtsogolo, ndinaŵerenga nkhani iriyonse m’magazine a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! ndi chisamaliro choposa chanthaŵi zonse zimene zinagogomezera pa mikhalidwe ya umunthu ndiyeno nkumawaika mu faelo. Ndinasunganso mosamalitsa nsonga zopangidwa mu Utumiki Waufumu zosonyeza mmene tingalankhuzanire ndi ena.
Chonulirapo changa choyamba chinali kuyesa kulankhuzana kwa nthaŵi yaitali monga mmene kukathekera ndi munthu mmodzi pa msonkhano Wachikrisitu uliwonse. Poyambayamba, kulankhuzana koteroko kunangotenga pafupifupi mphindi imodzi. Monga chotulukapo, nthaŵi zambiri ndinabwera kunyumba wodzimva wolephera. Komabe, mwakuumirira luso langa lakulankhuzana linawongokokera mwapang’onopang’ono.
Ndinayambanso kufufuza kwambiri mwaumwini pa mafunso ozunguza mutu amene ndinalinawo. Kuwonjezerapo, ndinapereka chisamaliro ku kadyedwe kanga kakuthupi ndi kupeza kuti mwakudya zakudya zopatsa thanzi, malingaliro anga ndi kaimidwe kathupi zinawongokera. Pambuyo pake ndinazindikira kuti zochititsa zina zingayambitse tondovi. Mwachitsanzo, nthaŵi zina ndinakhala wodziloŵetsa kwambiri m’chokondweretsa chinachake ndi kufikadi pa kumwerekera. Chimenechi mosapeŵeka chinanditsogoza ku kupsyinjika, kutulukapo kutaikiridwa nyonga kenaka kuchita tondovi. Yankho linali kuphunzira kukhala wopitirizabe kukondweretsedwa m’chinthu komabe nkusasangalatsidwa mopambanitsa. Kufikira lerolino, ndiyenera kuchenjera.
Sitepe lotsatira linali kupata chonulirapo chimene makolo anga nthaŵi zonse anatiikira monga ana, ndicho, uminisitala wanthaŵi zonse. Kufunitsitsa kwa mlongo wanga kompangitsa kugwirabe mwaŵi umenewu waupainiya kwa zaka zoposa 35 kukukhalabe chisonkhezero chabwino mwa ine.
Kuchita Ndi Vuto la Mwana Wanga
Pambuyo pa zaka zingapo monga mpainiya wosakwatira, ndinakwatira mpainiya mnzanga, Josefa. Iye wakhala wondithangata wabwino m’njira iriyonse. M’kupita kwanthaŵi, tinakhala ndi ana atatu. Craig, woyamba, anabadwa mu 1972 ali ndi manjenje owopsya. Vuto lake lakhaladi chitokoso, popeza kuti sakodza kudzichitira chiri chonse kusiyapo kungokandabzya chakudya ndi supuni. Indedi, timamkonda kwambiri, chotero ndinalondola njira zonse kumthandiza kumadzichitira zinthu mowonjezereka. Ndinamthandiza m’njira zosiyanasiyana kuti ayende. Tinafufuza akatswiri ambiri koma tinali ndi chipambano chochepa. Zandipangitsa kuzindikira kuti mikhalidwe ina m’moyo wake iyenera kulandiridwa.
Mkati mwa zaka 12 zoyambirira za moyo wake, Craig mwadzidzidzi ankaleka kudya ndi kumwa. Ichi chinatsagana ndi kugeya kosalekeza. Kuwonongeka kwa dongosolo la mitsempha kunalingaliridwa kukhala chochititsa. Iye pang’ono pang’ono ankayamba kuziririka m’maso mwathu. Pemphero linatithandiza kupirira, ndipo mankhwala operekedwa anathandiza kuchepetsa vutolo. Mwachimwemwe, Craig anawoneka kubweramo mphamvu m’kanthaŵi kochepa, ndipo kachiŵirinso akatisangalatsa ndi kumwetulira kwake kochititsa chidwi ndi nyimbo zake zosaleka.
Poyamba Josefa anakupeza kukhala kovuta kusinthira ku mkhalidwe wovutitsa umenewu. Koma chikondi chake ndi kuleza mtima m’kusamalira chosoŵa chirichonse cha Craig m’kupita kwa nthaŵi zinatha. Izi zatanthauza kuti takhala okhoza kupitirizabe kusamukira kulikonse kumene chosoŵa kaamba ka thandizo Lachikristu chiri chokulira. Ndi chirikizo la Josefa ndi thandizo logwira ntchito, ndinali wokhoza kuchita ntchito yapambali kwa zaka zingapo, kumandilola kuchita upainiya wothandizira limodzinso ndi kusamalira banja langa.
Kufunika kwa Kulingalira Kwabwino
Pamene Craig achita tondovi chifukwa cha kudwala kobwerezabwereza kapena kukhumudwitsidwa ndi zolephera zake, timamlimbikitsa ndi limodzi la malemba anga apamtima limene limati: “Si ndife a iwo akubwerera kuloŵa chitayiko.” (Ahebri 10:39) Iye amalidziŵa ilo pamtima, ndipo nthaŵi zonse limamlimbikitsa.
Popeza kuti Craig adakali wachichepere, iye wakhala ndi chikondi chapadera cha utumiki wakumunda. Mwakugwiritsira ntchito mpando wamagudumu wapadera, iye kaŵirikaŵiri amakhoza kutsagana nafe. Makamaka amakondwera kupita nafe pamene, nthaŵi ndi nthaŵi, ndimatumikira mipingo ina m’ntchito yothandizira mtumiki wadera. Ndemanga zake zochepa pa phunziro la gulu ndi kulankhula kwake kosaleka ponena za nkhani za m’Baibulo pa sukulu yapadera imene ankapitako, zinali ndi chisonkhezero chimene ife osapunduka sitinachipange. Motero Craig anandikumbutsa kuti mosasamala kanthu za zolephera zathu, Yehova angatigwiritsire ntchito kupititsa patsogolo chifuniro ndi cholinga chake.
Nthaŵi ina kale ndinali ndi mwaŵi wokhala mlangizi pa Sukulu Yautumiki Waufumu. Pambuyo pa zaka zanga zonse mu uminisitala, ndinali ndidakali ndi mantha poyamba. Koma posachedwapa, mwakudalira pa Yehova, mantha anga anatha, ndipo kachiŵirinso ndinadzimva kukhala ndi mphamvu yolimbikitsa ya Yehova.
Kuyang’ana kumbuyo pa zaka za moyo pafupifupi 50 tsopano, ndine wokhutiritsidwa kuti Yehova yekha ndiye angaphunzitse mwachikondi munthu wonga ine, kumsandutsa kukhala munthu wauzimu.