Anthu a ku Venezuela Aphunzira Kukhulupirira mwa Yehova
“ZAKA za Kuchuluka”—mmenemo ndi mmene anthu ambiri a ku Venezuela amakumbukirira nyengo yotsatira 1976. Chaka chimenecho, boma linakhala ndi umwini pa makampani onse amafuta a maiko akunja okhala mu Venezuela, ndipo chuma cha dzikolo chinakula. Monga umboni wa kuchuluka kwa zinthu zakuthupi kopezedwa chatsopano, maprojekiti omanga nyumba ambiri anayamba kuwonekera kuzungulira dzikolo. Zimango zazitali koposa m’dzikolo, Parque Central Towers, zinaimikidwa mu Caracas, mzinda waukulu. Anthu anawoneka kukhala ndi chifukwa chirichonse cha kuika chikhulupiriro chawo m’kupita patsogolo kosangalatsako.
Lerolino, ngakhale kuli tero, kawonedwe kakuwoneka kukhala kosalonjeza kwenikweni. Ngakhale kuti udakali mtundu wopita patsogolo, Venezuela yakhala ndi mbali yake ya mavuto a zachuma. Onse kuno amakumbukira ‘Lachisanu Lakuda,’ monga momwe February 28, 1983, imatchedwera mofala, pamene mphamvu ya ndalama yeniyeni, yotchedwa bolivar, inachepetsedwa. Monga chotulukapo, ndalamayo inataya mphamvu, ndipo ngongole za maiko akunja zinayamba kukula. Mwadzidzidzi, “Zaka za Kuchuluka” zinasinthira kukhala “Zaka za Kupereŵera.” Ambiri akhala ogwiritsidwa mwala kwakukulukulu ndi chidaliro chawo ndi chikhulupiriro zoikidwa pa malo olakwika. Mosiyanako, Mboni za Yehova mu Venezuela zaphunzira kuika chikhulupiriro chawo mwa Mulungu wowona, Yehova. Iwo asangalala ndi kukula kopitirizabe ndi kufutukuka mkati mwa zaka.
Kukula kwa Mbewu za Ufumu Zoyambirira
Munali mu 1936 pamene mbewu za mbiri yabwino ya Ufumu zinabweretsedwa kwa nthaŵi yoyamba ku Venezuela ndi apainiya aŵiri, kapena atumiki a nthaŵi zonse, ochokera ku Texas, U.S.A. (Mateyu 24:14) Zaka khumi pambuyo pake, amishonale aŵiri—omaliza maphunziro a kalasi lachisanu la Sukulu ya Gileadi ya Baibulo ya Watchtower—anafika. Ndipo mu September chaka chimenecho, ofesi ya nthambi ya Watch Tower Society inatsegulidwa mu Venezuela. Ripoti la chaka chimenecho linasonyeza chiwonkhetso cha olengeza Ufumu 19 mu Venezuela.
Mu November 1953, N. H. Knorr, yemwe anali prezidenti wa Sosaite pa nthaŵiyo, ndi mlembi wake, M. G. Henschel, anaima mu Venezuela pa ulendo wawo wochezera South America. Mazana asanu ndi anayi mphambu makumi anayi ndi aŵiri anabwera ku msonkhano wochitidwira mu Caracas. Podzafika mu 1977 chiŵerengero cha ofalitsa a Ufumu mu Venezuela chinakula kufika pa chiŵerengero chapamwamba cha oposa 13,800. Chimenecho chinachipangitsa icho kukhala choyenera kumanga ofesi ya nthambi yatsopano mu La Victoria, makilomita 85 kunja kwa likululo. Gawo latsopano linawonjezeredwa ndi kuperekedwa mu 1985. Lerolino, pali ofalitsa oposa 42,900 m’mipingo ndi magulu 500 mu Venezuela. Ndipo anthu ambiri owonjezereka mu Venezuela akuphunzira kuika chikhulupiriro chawo mwa Yehova, monga momwe zasonyezedwera ndi chiŵerengero cha opezekapo chabwino koposa cha 154,881 pa Chikumbutso cha imfa ya Kristu cha 1988.
Munda Wosiyanasiyana komabe Wachonde
Venezuela liri dziko la kusiyanasiyana, ndipo chimenechi chikuwunikiridwa mwa awo omwe aphunzira kuika chikhulupiriro chawo mwa Yehova. Choyamba, dziko limeneli limadziŵika kaamba ka obwera m’dziko ake ambiri. Chotero, ngakhale pakati pa Mboni za Yehova, pali ambiri ochokera ku Italy, Portugal, Germany, Spain, France, Haiti, Trinidad, Cuba, Dominican Republic, Ecuador, ndi malo ena. Komabe ali ogwirizana ndi anthu anzawo a ku Venezuela m’kukhulupirira ndi kutumikira Mulungu wowona, Yehova.
Palinso kusiyana kwambiri kwa magawo. Msodzi wa nsomba wa Kum’mawa wochokera ku zigawo za kum’mawa ali modziŵika wosiyana ndi woŵeta ng’ombe llanero wochokera ku zidikha za kum’mwera. Caraqueño woyenda mofulumira wochokera ku likulu, kapena wogwira ntchito pa kampani ya mafuta yemwe ali pafupi kuleka wochokera ku Maracaibo, mzinda waukulu wachiŵiri wa mtunduwo, ali a pawokha osiyana ndi mlimi woyenda pang’onopang’ono Andino wochokera kum’mwera chakumadzulo, kumene Mapiri a Andes amayambira. Aliyense ali ndi miyambo yake ndi katchulidwe ka mawu. Chotero, limodzi ndi ukoma wachilendo woperekedwa ndi obwera m’dzikomo, pali kusiyanasiyana kokongola pakati pa anthuwo.
Mosasamala kanthu za umoyo wakumbuyo wosiyanasiyana woterowo, anthu ochokera ku kakhalidwe konse ka moyo abwera kudzaphunzira ponena za Yehova. María Luisa anali mmodzi wa iwo. Chiyambire pamene iye anali wa zaka zakubadwa zisanu ndi ziŵiri, iye anakhala wodziloŵetsa m’kukhulupirira mizimu. Pamene anakula, iye anamwerekera m’zakumwa zoledzeretsa ndi anam’goneka, anatsogoza moyo wachisembwere, ndipo analoŵetsedwa m’kulambira mulungu wachikazi wa ku Venezuela María Lionza.a Atanyansidwa ndi njira yake ya moyo, iye anayamba ntchito m’mishoni ya Chikatolika pakati pa Amwenye kumbali ya kumadzulo kwa dzikolo. Iye mwamsanga anamaliza kuti ntchito yake sinali kuthandiza Amwenye osatinso ngakhale iye. Kenaka iye anayamba kufufuza m’nthanthi ya zenizeni za chilengedwe ndi m’kusinthasintha kwa moyo koma popanda phindu. Pa nsongayi, María Luisa anachezeredwa ndi Mboni za Yehova. Chidziŵitso cha Baibulo chomwe anapeza chinampatsa nyonga yomwe anafunikira kulimbana ndi mizimu yoipa. Tsopano iye akuika chikhulupiriro chake mwa Yehova ndipo ali wolengeza wa mbiri yabwino ya Ufumu wokangalika.
Ngakhale anthu olemala akuphunzira kuika chikhulupiriro chawo mwa Yehova, monga momwe ziriri ndi Juan ndi Carlos, abale aŵiri mwakuthupi. Pamene iye anali wa zaka zakubadwa zisanu ndi zinayi, Carlos anayambukiridwa ndi nthenda ya meningitis ndipo anakhala wakhungu. Pambuyo pake, ngakhale kuti anali wogwirizana ndi bungwe lochiritsa la Chikatolika, iye anayamba kuphunzira Baibulo ndi Mboni za Yehova. Iye anabatizidwa mu 1982, ndipo chiyambire December 1983 iye wakhala mtumiki wa nthaŵi zonse. Monga mpainiya wakhungu, iye amayenda ku ngodya iriyonse ya gawo lake, ali yekha pamene chiri chofunikira. Mbale wake Juan, ngakhale kuli tero, ali nkhani yosiyana kwenikweni.
Juan ali wa utali wa mamita 1.8 ndipo anali wandewu kwenikweni m’khwalala. Tsiku lina iye anawomberedwa mfuti kaŵiri mumsana. Ngakhale kuti anapulumuka, anasiidwa wakufa ziŵalo kuchokera m’chifuwa kutsika pansi ndipo anakhala wobindikiritsidwa pa kama kotheratu. Pamene Mboni zinamfikira, iye mozengereza analandira kudzipereka kwawo kwa kuphunzira Baibulo ndi iye. Maphunzirowo anadzutsanso ulemu wake kaamba ka Baibulo. Chiyembekezo cha moyo wangwiro m’Paradaiso chinamkhudza iye. Pambuyo pa kuleka kusuta, kumwa, ndi kugwiritsira ntchito chinenero choipa, mabwenzi ake akale onse anamsiya iye chifukwa, monga mmene iwo anachiikira icho, Juan anakhala “woyera.” Chikhalirechobe, iye anapitiriza kukhulupirira mwa Yehova, ndipo pomalizira anabatizidwa.
“Kukhala wobindikiritsidwa pa kama sikunandiletse ine kuchita chifuniro cha Yehova,” akutero Juan, “chifukwa ngakhale ziri tero manja anga ndi ubongo zikugwirabe ntchito bwino.” Ndimotani mmene iye amatumikira Yehova mu mkhalidwe wake? “Ndimagwiritsira ntchito tepirekoda yanga kukwaniritsa mathayo anga, onga ngati nkhani mu Sukulu ya Utumiki wa Teokratiki, mbali mu Msonkhano wa Utumiki, ndi kuŵerenga pa Phunziro la Nsanja ya Olonda la mlungu ndi mlungu. Ndiri ndi mwaŵi wa kutsogoza limodzi la Maphunziro a Bukhu pa Mpingo a kumaloko, lomwe limachitidwira panyumba yanga. Ndakhalanso wokhoza kutumikira monga mpainiya wokhazikika.” Ndimotani mmene iye akudzimverera ponena za zonsezi? “Ndiri wachiyamikiro kwambiri kwa achibale anga ndi abale ndi alongo anga auzimu, omwe ali othandiza chotero kwa ine. Ndiyembekeza ndi kupemphera kuti tonsefe tipirire m’kuika chikhulupiriro chathu mwa Yehova kotero kuti tikhoze kuwona pamene ‘opunduka adzatumpha ngati nswala.’”—Yesaya 35:6.
Misonkhano Ibweretsa Chitamando kwa Yehova
Kuti apitirize ndi ntchito yomwe ikuthandiza ambiri chotero kuika chikhulupiriro chawo mwa Yehova, Mboni mu Venezuela posachedwapa zamanga Maholo Osonkhaniramo aŵiri. Imodzi ya amenewa iri mu Campo Elias, Boma la Yaracuy, ku mbali ya kumadzulo koma chapakati pa dzikolo. Inayo, yokhazikitsidwa chifupifupi makilomita 60 kum’mwera kwa Caracas, iri yokonzekeretsedwa mokwanira ndi dziŵe la ubatizo, zoziziritsa ndi kutenthetsa mpweya, kitchini, ndi chipinda chodyeramo.
Maholo amenewa akondweretsa anthu akunja kwakukulu ndi okondwerera omwe abwera kudzawawona. Woyendetsa basi wina analembedwa ganyu ndi gulu la Mboni kuzipereka izo ku msonkhano wawo wadera. Pamene anafika ndi kuwona malo aakulu oimikapo magalimoto ndi malo ozungulira okongola, woyendetsayo analingalira kuti anayeneranso kupita mkati kuti awone malo amenewa. “Chomwe ndinawona mkati mwa Holo Yosonkhaniramo imeneyo chinali dziko lina, kufutukuka kwina,” iye anatero pambuyo pake. Iye anasangalatsidwa kwenikweni ndi dongosolo ndi umodzi kotero kuti anamvetsera mosamalitsa ku programu yonse. Pambuyo pake iye anafunsa kaamba ka phunziro la Baibulo ndipo tsopano ali mbale wobatizidwa.
Pa nthaŵi ina msonkhano wadera unayenera kuchitidwira mu El Tigre, mzinda ku mbali ya kum’mwera koma cha kum’mawa kwa dzikolo. Popeza kunalibe Holo Yosonkhaniramo m’dera limenelo, malo a kumaloko anabwerekedwa. Ngakhale kuli tero, chosadziŵika kwa abale, phwando la kusangalala linafunikira kuchitidwa mu mzinda umenewo pa madeti amodzimodziwo. Pamene aulamuliro a kumaloko anabwera kudzaika pulatiformu pambali penipeni pa malo a msonkhano, Mbonizo zinachonderera ndi olinganiza phwando la kusangalalalo kuti aike pulatiformuyo kwinakwake koma mosaphula kanthu. Monga kotembenukira komalizira, Mboni ina inawuza omwe anali oyang’anira kuti: “Chonde dziŵani kuti inu mukufunafuna vuto ndi Yehova.” Pakumva chimenechi, mwamuna woyang’anira anayankha kuti: “Oo, ayi, ine sindikufuna vuto ndi Yehova!” Kuchitidwa kwa phwando la kusangalalalo kunasamutsidwira ku malo ena patali ndi pamene msonkhano wadera unayenera kuchitidwira.
Pa msonkhano wina, mwamuna wa mlongo, mwamuna wokhala ndi ntchito ya ndale zadziko, anabwera kudzawona ngati mkaziyo anali kukhala ndi kachitidwe kena ndi winawake kumeneko. Iye anadabwitsidwa ndi mtundu wa nkhani zoperekedwa. “Ngati ndingalankhule mofanana ndi mwamuna uja, ndikakhozadi kupita patsogolo mu ntchito yanga ya ndale zadziko,” iye anawuza mkazi wake. Pambuyo pa programuyo, iye anafikira mmodzi wa akulu ndi kufunsa kuti asonyezedwe mmene angawongolere kulankhula kwake kwapoyera—ndipo kokha chimenecho. “Musandiyembekezere ine kupita ku khomo ndi khomo ndi chola,” iye anachenjeza tero. Phunziro la Baibulo linayambidwa, ndipo mwamsanga mwamunayo anasintha ganizo lake—iye anafuna kupita ku khomo ndi khomo ndi chola ndi kulalikira mbiri yabwino! Iye anasiya ndale zadziko ndi kubatizidwa, ndipo tsopano iye ndi banja lake amaika chikhulupiriro chawo mwa Yehova.
Kupanga Njira kaamba ka Kufutukuka Kowonjezereka
Mkati mwa kuchezera kwa L. A. Swingle, chiŵalo cha Bungwe Lolamulira la Mboni za Yehova, khamu la 63,580 linasonkhana m’bwalo lolimbanirana ng’ombe zamphongo la Plaza Monumental mu Valencia. Ambiri a iwo anayenda ndi basi usiku wonse. Onse opezekapo analimbikitsidwa kwambiri kumva Mbale Swingle akuwawuza kuti: “Inu simulinso nthambi yaing’ono. Tsopano inu muli nthambi ya ukulu wapakati. Ndipo mwa mawonedwe ake, tsiku lina posachedwa inu mudzakhala mu ‘gulu lokhala ndi ofalitsa 100,000’!”
Makonzedwe akupangidwa kufutukula ofesi ya nthambi mu La Victoria kusamalira kaamba ka kukula kodabwitsa. Inde, mwa zikwizikwi, anthu mu Venezuela akuphunzira kukhulupirira mwa Yehova.
[Mawu a M’munsi]
a Onani Galamukani! ya June 22, 1967, masamba 21-3, m’Chingelezi.
[Mapu/Chithunzi patsamba 21]
(Onani m’magazini yeniyeni kuti mumvetse izi)
CARIBBEAN SEA
VENEZUELA
Maracaibo
ANDES MOUNTAINS
Campo Elias
Valencia
La Victoria
Caracas
El Tigre
COLOMBIA
BRAZIL
GUYANA
600 Km
400 mi
[Zithunzi patsamba 24]
Kawonedwe ka malo akunja ndi amkati a Holo Yosonkhaniramo ya Cúa