Chothandizira Kuphunzitsa Chozizwitsa
MWANA wachichepere angakumbukire zoposa zimene mumalingalira. Mu kalata ya chiyamikiro kaamba ka makaseti tepi a Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo, (Chingelezi) mayi wochokera ku Florida (U.S.A.) akulemba ponena za mwana wake wamwamuna wa zaka zisanu zakubadwa:
“Ngati mumufunsa iye kokha ndi nambala, iye amadziŵa chimene nkhaniyo imanena. Iye sanadziŵebe kuŵerenga koma waloweza nkhanizo ndipo angazinene izo pa mtima. Anthu andiuza ine kuti ana awo sangapite kukagona popanda bulangeti kapena zoseŵeretsa. Wanga sangagone popanda choseŵerera tepi chake chotsegulidwa. Iye amamvetsera ku nkhanizo nthaŵi zonse. Iye amagona usiku uliwonse akumvetsera ku izo. Pano pali chithunzi chake akumvetsera ku izo.”
Kumvetsera ku makaseti a nkhani 116 mu Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo kudzathandiza achichepere anu kuphunzira chimene Baibulo limanena. Kodi mukugwiritsira ntchito chothandizira kuphunzitsa chabwino kwambiri chimenechi? Alubamu yokhala ndi makaseti anayi iri kokha K64; nthaŵi yoseŵerera maora asanu ndi theka.
Chonde tumizani, mutalipiriratu positi, alubamu ya brown vinyl yokhala ndi makaseti tepi anayi a Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo (Chingelezi). Ndatsekeramo K64 (Zambia). (Kunja kwa Zambia, lemberani ofesi ya nthambi ya Watch Tower ya kwanuko kaamba ka mtengo.)