Mawu a M'munsi
a Yosefe anatchulidwa komaliza pamene Yesu anali ndi zaka 12. Pa nthawi imene Yesu anachita chinthu chodabwitsa choyamba, chomwe ndi kusandutsa madzi kukhala vinyo, Yosefe sanatchulidwe ndipo satchulidwanso munkhani zina zotsatira. Ndipo Yesu ali pamtengo wozunzikirapo, anauza mtumwi Yohane kuti azisamalira mayi ake. Akanakhala kuti Yosefe anali moyo, Yesu sakananena zimenezi.—Yoh. 19:26, 27.