Mawu a M'munsi
a Chiŵerengero chenicheni cha asilikali ndi anthu wamba omwe afa sichikudziŵika. Mwachitsanzo, buku la 1998 lakuti Facts About the American Wars (Zoona Zake za Nkhondo za America) linanenapo za nkhondo yachiŵiri yokha yadziko lonse kuti: “Mabuku ambiri amapereka chiwonkhetso cha omwe anafa pa nkhondo yachiŵiri ya padziko lonse (asilikali ndi anthu wamba) kukhala 50 miliyoni koma ambiri omwe afufuza mosamalitsa nkhaniyi akukhulupirira kuti chiŵerengero cholondola n’chokwera kwambiri, ngakhale kuŵirikiza kaŵiri nambala imeneyo.”