Mawu a M'munsi
c Kumeneku kunali kuphonya kumene mipingo yambiri ya Dziko Lachikristu inachita. Lutheran linali dzina lowajeda nalo limene adani a Martin Luther anapatsa otsatira ake, amenenso analilandira. Mofananamo, a Baptist analandira dzina lowajeda nalo limene akunja anawapatsa chifukwa chakuti iwo ankalalikira ubatizo wa kumiza. Mofanananso ndi zimenezo, zichita ngati kuti a Methodist analandira dzina limene akunja anawapatsa. Ponena za mmene a Society of Friends anafikira pa kutchedwa Quakers, The World Book Encyclopedia imati: “Liwulo Quaker poyamba linali lotonza Fox [myambitsi wake], amene anauza woweruza Wachingelezi ‘kunthunthumira ndi Mawu a Ambuye.’ Woweruzayo anatcha Fox ‘quaker.’”