Mawu a M'munsi
f Profesa Walter L. Liefeld akulemba kuti: “Nkothekadi kunena kuti maulosi a Yesu anali ndi mbali ziŵiri: (1) zochitika za mu A.D. 70 zokhudza kachisi ndi (2) zamtsogolo kwambiri, zofotokozedwa m’mawu olosera kwambiri.” Buku la ndemanga lokonzedwa ndi J. R. Dummelow limati: “Zambiri za zovuta zazikulu za m’nkhani yaikulu imeneyi zimatha pamene tizindikira kuti Ambuye wathu sanangotchula chochitika chimodzi koma ziŵiri, ndi kuti choyamba chinali kuphiphiritsira chachiŵiri. . . . Makamaka lemba la [Luka] 21:24, limene limanena za ‘nthaŵi za Akunja,’ . . . limaika nthaŵi yautali wosadziŵika pakati pa kugwa kwa Yerusalemu ndi mapeto a dziko.”