Mawu a M'munsi
b Kwa zaka zambiri Nsanja ya Olonda inalingaliridwa kukhala magazini a Akristu odzozedwa okha. Komabe, kuyambira mu 1935, chigogomezero chowonjezereka chinaperekedwa pa kulimbikitsa a “khamu lalikulu,” amene chiyembekezo chawo ndicho moyo wosatha padziko lapansi, kutenga ndi kuŵerenga Nsanja ya Olonda. (Chivumbulutso 7:9) Patapita zaka zingapo, mu 1940, Nsanja ya Olonda inali kugaŵiridwa nthaŵi zonse kwa anthu m’makwalala. Zaka zingapo pambuyo pake, chiŵerengero cha makope ofalitsidwa chinawonjezereka mofulumira.