Mawu a M'munsi
a Zina za nyimbo zaposachedwapa zingakhale zovutirapo pang’ono kwa ife kuziimba choyamba, koma pambuyo pa kuzoloŵerana nazo, izo zingatsimikizire kukhala zokondedwa zathu za pamtima. Mwachitsanzo, pamene bukhu la nyimbo lapapitapo linabwera, nyimbo 88, “Kuyenda mu Umphumphu,” siinakondedwe mu dziko lina, koma pambuyo pake iyo inakhala nyimbo yokondedwa kwambiri.