Mawu a M'munsi
c Mfundo imodzi imene inachititsa kuti machenjezo ngati amenewa akhale opanda mphamvu inali yakuti machenjezowa kwenikweni ankapita kwa kagulu ka nkhosa ka 144,000. M’mutu 5 tidzaona kuti chisanafike chaka cha 1935, anthu ankakhulupirira kuti “khamu lalikulu” lofotokozedwa pa Chivumbulutso 7:9, 10, lidzapangidwa ndi anthu ambirimbiri a m’matchalitchi amene amati ndi achikhristu. Gulu limeneli lidzakhala gulu lachiwiri limene lidzalandire mphoto yawo kumwamba chifukwa chogwirizana ndi Khristu ngakhale kuti adzachita zimenezi nthawi itatha kale.