Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w26 February tsamba 26-29
  • Ana Ndi “Cholowa Chochokera kwa Yehova”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ana Ndi “Cholowa Chochokera kwa Yehova”
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2026
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • MAVUTO OMWE AMAKHALAPO
  • KODI YEHOVA AMAFUNA KUTI MAKOLO AZICHITA CHIYANI?
  • YEHOVA NDI WOFUNITSITSA KUKUTHANDIZANI
  • Makolo Ayenera Kuphunzitsa Ana Awo Kukonda Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Makolo, Muzithandiza Ana Anu Kuti Azikonda Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
  • Makolo, Pezerani A M’banja Lanu Zosowa Zawo
    Nsanja ya Olonda—2005
  • Makolo—Kodi Ana Anu Akukula Mwauzimu?
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2026
w26 February tsamba 26-29
Bambo ndi mayi akumbatira mwana wawo wamkazi ndipo akuoneka osangalala.

Ana Ndi “Cholowa Chochokera kwa Yehova”

KODI n’chiyani chimene chimabwera m’maganizo mwanu mukamva mawu akuti “cholowa”? Kodi ndi ndalama, malo kapena nyumba kapenanso chinthu chinachake chamtengo wapatali chimene munalandira kuchokera kwa anthu a m’banja lanu? Kaya cholowa chake ndi chotani, chimakhalabe chamtengo wapatali ndipo mumafunitsitsa kuchisamalira.

Baibulo limati ana ndi “cholowa chochokera kwa Yehova.” (Sal. 127:3) Choncho n’zosachita kufunsa kuti makolo a Chikhristu amaona kuti ana awo ndi mphatso zochokera kwa Atate wawo wakumwamba ndipo amayesetsa kuwateteza komanso kuwasamalira. Amafunanso kuwathandiza kuti azisangalala komanso akhale pa ubwenzi wabwino ndi Yehova.

Koma n’zomvetsa chisoni kuti masiku ano makolo ena saona kuti ana awo ndi cholowa chochokera kwa Mulungu. (Yes. 49:15; 2 Tim. 3:​1-3) Ena angamafunitsitse kusamalira ana awo koma zimawavuta kuchita zimenezi chifukwa cha mavuto osiyanasiyana. Kodi ena mwa mavuto amenewa ndi ati? Kodi Yehova amafuna kuti makolo azitani? Nanga kodi makolo angatani kuti alere bwino ana awo?

MAVUTO OMWE AMAKHALAPO

  • Zimene achibale komanso ena amayembekezera. M’madera ena, anthu amalemekeza kwambiri makolo omwe ali ndi ana ochuluka. Choncho anthu okwatirana angamakakamizidwe ndi achibale kapena maneba kuti akhale ndi ana ambiri, mwinanso kuposa omwe angathe kuwasamalira.

  • Kudera nkhawa zam’tsogolo. M’mayiko amene ana ambiri amamwalira chifukwa cha kuperewera kwa zakudya m’thupi, matenda komanso kusowa kwa thandizo la zaumoyo, mabanja ena amakhala ndi ana ambiri n’cholinga choti ngati ana ena atamwalira, padzapezeke ena opulumuka. Makolo enanso angasankhe kukhala ndi ana ambiri kuti akadzakalamba anawo adzawasamalire. Zimenezi zimachitika kwambiri m’mayiko amene boma silipereka thandizo kwa achikulire.

  • Njira za kulera. M’madera ena, sizikhala zophweka kuti mabanja apeze mankhwala othandiza kuti mayi asatenge mimba. Pomwe ena amada nkhawa kuti thupi lawo siligwirizana ndi njira zakulera zosadalirika zomwe zimapezeka m’dera lawo. Ndiye pali enanso amene sangathe kugwiritsa ntchito njira za kulera chifukwa choti ndi zodula.a

KODI YEHOVA AMAFUNA KUTI MAKOLO AZICHITA CHIYANI?

Banja lapita kukasangalala kumalo enaake okongola. Bambo akumvetsera mwatcheru pamene mwana wake wamkazi akufotokoza maganizo ake, pamene mayi akusewera mpira ndi mwana wake wamwamuna.

Muzipeza nthawi yochita zinthu ndi mwana aliyense payekha

Muzipezera ana anu zomwe amafunikira. Yehova anapatsa makolo udindo wopezera ana awo aang’ono zimene amafunikira. Iye amayembekezera kuti makolo azigwira ntchito mwakhama kuti apezere mwana aliyense chakudya, zovala komanso malo ogona. Yehova amafunanso kuti makolo azionetsetsa kuti anawo aphunzira zinthu zimene zingadzawathandize. Choncho makolo a Chikhristu samangofulumira kutumiza ana awo kumasukulu ogonera komweko. Koma amaonetsetsa kuti anawo akukhalabe panyumba mpaka atakula n’cholinga choti aphunzire maluso omwe angawathandize pa moyo. Amapezanso nthawi yochita zinthu ndi mwana aliyense, zomwe zimamuthandiza kumva kuti ndi wotetezeka ndiponso amakondedwa. Komabe, Yehova ndi wololera ndipo sayembekezera kuti makolo akhale olemera kuti akwanitse udindowu. Ndipotu iye anasankha makolo amene anali olimbikira ntchito koma osauka kuti alere Mwana wake wokondedwa.—Mat. 13:​55, 56; Luka 2:24.

Mfundo ya m’Baibulo: “Ndithudi, ngati munthu sasamalira anthu amene ndi udindo wake kuwasamalira, makamaka a mʼbanja lake, wakana chikhulupiriro ndipo ndi woipa kuposa munthu wosakhulupirira.”—1 Tim. 5:8.

Yehova amamvetsa kuti makolo angamafunike kuthandizidwa pamene akukula. Ndipotu njira ina imene ana angalemekezere makolo awo ndi kuwathandiza pamene akalamba. (Eks. 20:12; 1 Tim. 5:4) Komabe, Yehova amasangalala makolo akamaganizira kwambiri mmene adzasamalire anawo, osati mmene anawo adzasamalire makolowo.—2 Akor. 12:14.

Muziwathandiza mwauzimu. Makolo alinso ndi udindo wophunzitsa ana awo kuti azikonda komanso kulambira Yehova. Iye amaona kuti zimenezi ndi zinthu zofunika kwambiri zomwe makolo ayenera kuphunzitsa ana awo.—Deut. 6:​6, 7.

Mfundo ya m’Baibulo: “Pitirizani kuwalera [ana anu] powapatsa malangizo komanso kuwaphunzitsa mogwirizana ndi zimene Yehova amanena.”—Aef. 6:4.

YEHOVA NDI WOFUNITSITSA KUKUTHANDIZANI

Mwamuna ndi mkazi ali m’nyumba akukambirana. Patebulo pali Baibulo lotsegula.

Muzikambirana kuchuluka kwa ana amene mukufuna kudzakhala nawo

Muziganizira zam’tsogolo. Ngati mukufuna kudzakhala ndi ana, muziganizira mofatsa mmene zinthu zilili pa moyo wanu. Mwachitsanzo, ngati mutadzakhala ndi ana ambiri, kodi muzidzakwanitsa kuwapezera chakudya, zovala ndiponso kuwapititsa kusukulu? Ngati si choncho, kambiranani ndi mwamuna kapena mkazi wanu n’kuona kuchuluka kwa ana omwe mungadzakhale nawo kuti muzidzakwanitsa kuwasamalira mmene Yehova amafunira. N’zoona kuti Yehova amamvetsa kuti tikhoza kukumana ndi zosayembekezereka pa moyo. (Mlal. 9:11) Komabe iye adzadalitsa zimene mukuyesetsa kuchita kuti mukhale makolo abwino.

Mfundo za m’Baibulo: “Mapulani a munthu wakhama amamuthandiza kuti zinthu zimuyendere bwino, koma onse amene amachita zinthu mopupuluma amasauka.”—Miy. 21:5.

“Ndi ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja sayamba wakhala pansi nʼkuwerengera ndalama zimene adzawononge, kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kumalizira nsanjayo?”—Luka 14:28.

Muziika Yehova pamalo oyamba m’banja mwanu. Kulambira Yehova kuzikhala chinthu chofunika kwambiri. Ngati muli ndi ana kale, muziyesetsa kuphunzitsa mwana aliyense payekha kuti azikonda Yehova. Muziwathandiza kuti azimvetsera mwatcheru pamisonkhano ya mpingo. Muzionetsetsa kuti mukuchita Kulambira kwa Pabanja wiki iliyonse. Muziphunzitsa ana anu kulalikira. Musamasiye udindo wolera ana m’manja mwa ana anu akuluakulu kapenanso achibale ena. Kuphunzitsa ana kuti azikonda Yehova kumafuna nthawi komanso khama, koma madalitso amene mumapeza amakhala ambiri.

Mfundo ya m’Baibulo: “Palibe chimene chimandisangalatsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akuyendabe mʼchoonadi.”—3 Yoh. 4.b

Muzidalira Yehova. Kaya mukuganizira zokhala ndi ana kapena muli nawo kale, musamakayikire kuti mfundo za Yehova n’zofunika kwambiri kuposa chikhalidwe kapena miyambo ya m’dera lanu.

Chithunzi: 1. Makolo akhala limodzi ndi mwana wawo wamwamuna pamisonkhano ya mpingo. Mwanayo waimika dzanja kuti apereke ndemanga. 2. Banja likuyendera limodzi mu utumiki. Bambo akuyenda ndi mwana wamkazi pamene mayi akuyenda ndi mwana wamwamuna.

Kuthandiza ana anu kuti akhale pa ubwenzi wabwino ndi Yehova, kumafuna nthawi komanso khama

Ngati mutasankha kukhala ndi ana ochepa, musamakayikire kuti Yehova azidzakupatsani zonse zofunika mukadzakalamba. Muzipewa maganizo oti ana ndi “podzapulumukira.” Musamaope kuti mudzasowa mtengo wogwira. Yehova akulonjeza kuti adzakusamalirani. Ndipotu nthawi zonse amakwaniritsa zimene walonjeza.—Yos. 23:14.

Mfundo za m’Baibulo: “Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, ndipo usamadalire luso lako lomvetsa zinthu. Uzimukumbukira mʼnjira zako zonse, ndipo iye adzawongola njira zako.”—Miy. 3:​5, 6.

“Ndinali mwana ndipo tsopano ndakula, koma sindinaonepo munthu aliyense wolungama atasiyidwa, kapena ana ake akupemphapempha chakudya.”—Sal. 37:25.

“Choncho nthawi zonse muziika Ufumu ndi mfundo zolungama za Mulungu pamalo oyamba pa moyo wanu, ndipo iye adzakupatsani zinthu zina zonsezi.”—Mat. 6:33.

Ana ndi mphatso yamtengo wapatali imene Yehova wapereka kwa makolo. Iye amasangalala makolo a Chikhristu akamalera ana m’njira imene iyeyo amafuna. Iwo amapezera ana awo zimene amafunikira, kuwathandiza kuti azisangalala komanso kuwathandiza mwauzimu. Amasankhanso kuchuluka kwa ana amene angakhale nawo ndipo amaona kuti zimene Mulungu amafuna n’zofunika kwambiri kuposa chikhalidwe kapena miyambo ya m’dera lawo. Makolo a Chikhristu akamachita zimenezi, amasonyeza kuti ana awo ndi mphatso yamtengo wapatali, kapena kuti “cholowa chochokera kwa Yehova.”

Sanong’oneza Bondo

Bambo ali ndi mkazi komanso ana ake awiri ndipo akuchititsa kulambira kwa pabanja.

Kodi makolo amakumana ndi mavuto chifukwa choti asankha kukhala ndi ana ochepa? Limeneli ndi funso limene makolo ambiri m’mayiko osauka amadzifunsa. Taonani zimene abale ena a m’mayikowa, omwe ndi mitu ya mabanja ananena.

Kodi anthu ena ankakukakamizani kuti mukhale ndi ana ambiri?

“Inde, ngakhalenso ena mumpingo. Banja lina linatifunsapo kuti, ‘N’chifukwa chiyani munangobereka mwana mmodzi yekha basi? Ku Africa kuno ukakhala ndi mwana mmodzi, zimangokhala ngati ulibe mwana. Ndipo ukakhala ndi ana awiri, zimangokhala ngati uli ndi mmodzi.’ Ngakhale pamene tinabereka mwana wathu wachiwiri wamkazi, anthu ankatilimbikitsabe kuti tibereke ana ena.”—Jeremias

Kodi munakumana ndi mavuto chifukwa chosankha kuti mukhale ndi ana ochepa?

“Ayi ndithu. Ndipotu chifukwa chosankha kukhala ndi ana ochepa, ine ndi mkazi wanga tinkakwanitsa kupeza zofunika pa moyo. Koposa zonse, tinkakwanitsa kuchita zinthu zomwe zikanatithandiza kukhala pa ubwenzi wabwino ndi Yehova. Ndinaleredwa m’banja lomwe munali ana ambiri ndipo ndinkaona mmene mayi ndi bambo athu ankavutikira kutipezera zinthu zofunika pa moyo komanso kutipititsa kusukulu.”—Jeremias

Kodi ana anu amamva bwanji pa zimene munasankhazi?

“Ana athu amasangalala chifukwa chakuti sanakumane ndi mavuto ngati ana ena, amene makolo awo ankavutika kuwasamalira chifukwa chokhala ndi ana ambiri.”—Filipe

“Pamene ankakula, iwo ankasangalala chifukwa chomva kuti ndi otetezeka komanso amakondedwa. Nthawi zambiri tinkaitana abale ndi alongo olimba mwauzimu omwe ankatilimbikitsa kuti tikhale ndi zolinga zauzimu. Masiku ano timasangalala kuona ana athu akutengera chitsanzo chawo chabwino.”—Carlos

Kodi kusankha kuti mukhale ndi ana ochepa kunakuthandizani bwanji?

“Chifukwa chosankha kuti tikhale ndi ana ochepa, tinkakwanitsa kusamalira bwinobwino banja lathu. Ntchito yamalipiro ambiri yomwe ndinkagwira inandithera pafupifupi zaka zitatu zapitazo. Sitinavutike kwambiri zinthu zitasintha chonchi chifukwa choti banja lathu linali laling’ono ndipo sitinkafunikira zinthu zambiri.”—Jeremias

“Zimene tinasankha zathandiza kuti tizipezera ana athu zinthu zofunika komanso kuwathandiza kuti akhale pa ubwenzi wabwino ndi Yehova. Kuwonjezera pamenepo, tinakwanitsa kukatumikira kumadera omwe kunkafunikira olalikira ambiri. Zimakhalanso zosavuta kusamalira mwana aliyense payekha. Ana athu onse akutumikira Yehova ndipo akuyesetsa kukwaniritsa zolinga zawo zauzimu.”—Lenadi

Mungapereke malangizo otani kwa makolo ena?

“Ndaona kuti mawu a pa Salimo 34:10b ndi oona, omwe amati: ‘Anthu amene akufunafuna Yehova sadzasowa chilichonse chabwino.’ Yehova wakhala akuthandiza ine ndi banja langa kupeza zonse zimene timafunikira.”—Rafael

a Mwamuna ndi mkazi wake ndi amene ayenera kusankha kuchuluka kwa ana amene adzakhale nawo, nthawi imene adzakhale ndi anawo komanso njira ya kulera imene adzagwiritse ntchito, bola ikhale yosachotsa mimba. Palibe amene ayenera kuwaweruza pa zimene asankha. (Aroma 14:​4, 10-13) Mabanja a Chikhristu amayeneranso kukumbukira malangizo a pa 1 Akorinto 7:​3-5.

b Ngakhale kuti ana otchulidwa pavesili ndi Akhristu amene Yohane anawaphunzitsa choonadi, ndi mmenenso makolo amamvera akaganizira za ana awo omwe akutumikira Yehova.

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena