Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w26 June tsamba 32
  • Maukonde Otchulidwa M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Maukonde Otchulidwa M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2026
  • Nkhani Yofanana
  • Kutumikira Monga Asodzi a Anthu
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Yesu Anaitana Ophunzira Ake 4
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Ophunzira Anayi Aitanidwa
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Moyo wa Anthu Akale—Msodzi
    Nsanja ya Olonda—2012
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2026
w26 June tsamba 32

ZINTHU ZOCHITITSA CHIDWI ZA M’BAIBULO

Maukonde Otchulidwa M’Baibulo

Anthu amene amawerenga Baibulo amadziwa kuti ena mwa otsatira a Yesu anali asodzi. (Maliko 1:​16-20) Iwo ankagwiritsa ntchito maukonde akamapha nsomba m’Nyanja ya Galileya.

Maukonde ankapangidwa poluka twayini kapena ulusi. Kukula kwa mabowo a maukondewa, kunkatengera mtundu wa nsomba zomwe akufuna kugwira. Nthawi zambiri kunsi kwa maukonde ang’onoang’ono ankamangirirako mwala kapena zinthu zina zolemera kuti maukondewa azitha kumira. Pamene maukonde akuluakulu ankakhala ndi zinthu zolemera kunsi ndipo pamwamba pake pankakhala zinthu zoti zitha kuyandama monga timatabwa.

Maukonde anali odula. Ankatha kung’ambika chifukwa cha miyala ya pansi pa nyanja kapena kuchuluka kwa nsomba zimene asodzi agwira. (Luka 5:6) Baibulo limanena kuti nthawi ina Yakobo ndi Yohane ‘ankasoka maukonde awo.’ N’kutheka kuti ankagwiritsa ntchito singano wamkulu ndi ulusi. (Mat. 4:21) Asodzi ayenera kuti ankachita zimenezi akabwera kopha nsomba. Luka anafotokozanso kuti asodzi “ankachapa maukonde awo” kuti achotse matope. (Luka 5:2) Pambuyo pake ankawayanika n’cholinga choti asawole.—Ezek. 47:10.

Yesu anaitana anthu amene ankadziwa bwino ntchito yausodzi kuti akhale “asodzi a anthu.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena