MUNTHU WOTCHULIDWA M’BAIBULO
Obadiya—Phunzirani Kuopa Mulungu
Obadiya anali woyang’anira nyumba ya mfumu yoipa Ahabu, yomwe inalola kuti kulambira Baala kufalikire mu Isiraeli. Komabe Obadiya anaphunzira kuopa Yehova ‘kuyambira ali mwana.’ (1 Maf. 18:1-13) Ndiye Mfumukazi Yezebeli italamula kuti aneneri onse a Yehova aphedwe, Obadiya anadziwa kuti ayenera kuchita zinthu molimba mtima kuti zimenezi zisachitike. Zinali zoopsa kungobisa ngakhale mneneri mmodzi, koma Obadiya anabisa aneneri 100 n’kumawapatsa chakudya pa nthawi imenenso kunali njala yaikulu. Sizinalitu zophweka kuti aneneri abodza mahandiredi omwe ankatumikira mfumu ndi mfumukazi asadziwe zimenezi.—1 Maf. 18:19.
Kodi tingaphunzire chiyani kwa munthu yemwe anali woopa Mulunguyu? Ngakhale kuti Obadiya ankachita mantha ndi Ahabu, iye ankaopa kwambiri Mulungu. Zimenezi zinamuthandiza kuti alimbe mtima n’kuika moyo wake pangozi kuti ateteze abale ake. Ngati ntchito yathu ndi yoletsedwa m’dziko limene tikukhala, ifenso tiyenera kuyesetsa kuti tiziopa Mulungu. Mantha amenewo adzatithandiza kukhala olimba mtima kuti tizithandiza abale ndi alongo athu amene akukumana ndi mavuto.