Zochitika mu Utumiki Wakumunda
M’mwezi wa September 2013, alongo 9 ochokera mu mpingo wa Lilongwe English anapita kukalalikira m’gawo la mpingo wa Ntcheu Central kwa mlungu umodzi ataloledwa ndi ofesi ya nthambi. Alongowa ankayamba kulalikira 5:30 m’mawa mpaka 6:30 madzulo. Pa mlungu umene anakhala kumeneku, analalikira maola 625 ndipo anagawira magazini 4,048. Alongowa anayamikira kwambiri mmene abale ndi alongo a mpingo wa Ntcheu Central anawathandizira polowa nawo mu utumiki komanso pa zinthu zina. Zimene alongowa anachita ndi zogwirizana ndi zimene timawerenga pa Salimo 110:3 kuti: “Anthu ako adzadzipereka mofunitsitsa pa tsiku limene udzatsogolera asilikali ako kunkhondo.” Apa zikuonekeratu kuti mtima wodzipereka ndi chizindikiro cha Akhristu oona.