Zilengezo
◼ Mabuku ogawira mu October: Magazini ya Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Ngati munthu ali ndi chidwi, gawirani ndi kukambirana kapepala kakuti Kodi Mukufuna Kudziwa Choonadi? n’cholinga choyambitsa phunziro la Baibulo. November: Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? Yesetsani kuyambitsa phunziro la Baibulo. December: Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako. Ngati anthu anena kuti ali ndi ana, agawireni buku la Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso. January 2009: Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
◼ Mwezi wa November ndi mwezi wabwino kwambiri kuchita upainiya wothandiza chifukwa chakuti uli ndi masiku asanu a Loweruka ndi Lamlungu.
◼ Mawu kwa woyang’anira wotsogolera ndi woyang’anira Sukulu ya Utumiki wa Mulungu: Ndandanda ya tsopano ya misonkhano ya mpingo iyamba kugwira ntchito mlungu woyambira December 29, 2008 ndipo tidzasonyeza kusinthaku mu Utumiki Wathu wa Ufumu wa December 2008. Panthawi ya Kubwereza za m’Sukulu ya Utumiki wa Mulungu, onetsetsani kuti mukutsatira malangizo amene ali mu Ndandanda ya Sukulu ya Utumiki wa Mulungu ya 2009 yomwe tatumiza limodzi ndi Utumiki Wathu wa Ufumu uno. Patsiku limeneli sipadzakhala luso la kulankhula.