Bokosi la Mafunso
◼ Kodi zingakhale zoyenera kukonza zoti anthu agulitse katundu wosiyanasiyana kapena achite zinthu zina zofuna kupezera ndalama n’cholinga chothandiza mpingo?
Si zachilendo kuti zipembedzo zikonze zinthu zopezera ndalama, monga kuphika zakudya, kugulitsa malonda, kapena kukonza zionetsero. Ngakhale kuti ena angaone kuti zinthu zimenezi n’zothandiza, kwenikweni imeneyi ndi mitundu ya kupemphetsa ndalama. Mboni za Yehova sizipeza ndalama m’njira imeneyo.
Magazini yachiwiri ya Watch Tower, ya August 1879, inanena mawu otsatirawa pofotokoza chifukwa chimene timakanira kutsanzira matchalitchi pankhani ya kupemphetsa ndalama: “Tikukhulupirira kuti amene akuyendetsa magazini ya ‘Zion’s Watch Tower’ ndi YEHOVA, ndipo kwa nthawi yonse imene zimenezi zidzakhale choncho, sidzapempha kapena kuchonderera anthu kuti aipatse ndalama. Iye amene ananena kuti: ‘Golide ndi siliva yense wa m’mapiri ndi wanga’ akadzalephera kupereka ndalama zofunikira, tidzadziwa kuti nthawi yoti tisiye kulemba magaziniyi yakwana.”
Timapitirizabe kumvera mfundo ya m’Malemba yakuti: “Aliyense achite mwa kutsimikiza kwa mtima wake, osati monyinyirika kapena mokakamizika ayi, pakuti Mulungu amakonda wopereka mokondwera.” (2 Akor. 9:7) Mabokosi a zopereka amaikidwa m’Nyumba ya Ufumu kuti anthu athe kupereka ndalama mwakufuna kwawo. (2 Maf. 12:9) Sitichita kupemphetsa zopereka, ndiponso siziperekedwa n’cholinga chopezapo kenakake.