Kubwereza za M’Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
Mafunso otsatirawa mudzawakambirana pa Sukulu ya Utumiki wa Mulungu ya mlungu woyambira December 25, 2006. Woyang’anira sukulu adzatsogolera kubwereza nkhani zomwe zakambidwa m’kati mwa milungu ya November 6 mpaka December 25, 2006. Kubwerezaku kudzakhala kwa mphindi 30. [Dziwani izi: Pa funso lomwe kumapeto kwake silikusonyeza buku lililonse lomwe mwatengedwa nkhaniyo, ndiye kuti muyenera mufufuze nokha kuti mupeze mayankho ake.—Onani buku la Sukulu ya Utumiki, mas. 36-7.]
LUSO LA KULANKHULA
1. Kodi n’chiyani chiyenera kutitsogolera tikamasankha mawu otchulira lemba? [be-CN tsa. 148 ndime 4–tsa. 149 ndime 1]
2. Kodi njira zina zimene tingagwiritse ntchito kuti titsindike bwino mawu athu n’ziti? [be-CN tsa. 151 ndime 4–tsa. 152 ndime 3]
3. Popeza kuphunzitsa ena Mawu a Mulungu ndi nkhani yaikulu kwambiri, kodi n’chiyani chimafunika kuti ‘tilunjike nawo bwino mawu a choonadi’? (2 Tim. 2:15) [be-CN tsa. 153 ndime 1-4, bokosi; tsa. 154 ndime 1]
4. Kodi tingatani kuti tigwiritse ntchito moyenera malemba amene tikuwerenga? [be-CN tsa. 154 ndime 3–tsa. 155 ndime 2]
5. Kodi n’chifukwa chiyani m’pofunika kwambiri kumveketsa phindu la nkhani yathu, ndipo njira zina zomwe tingachitire zimenezi n’ziti? [be-CN tsa. 157 ndime 1-5, bokosi]
NKHANI NA. 1
6. Kodi woyang’anira utumiki pa mpingo amakhala ndi udindo wofunika wotani potithandiza kukwaniritsa ntchito yathu yolalikira uthenga wabwino? [od-CN tsa. 41 ndime 3]
7. Kodi munthu aliyense akhoza kupatsidwa thandizo lotani kudzera m’makonzedwe a Phunziro la Buku la Mpingo? [od-CN tsa. 44 ndime 3]
8. Kodi cholinga chimodzi chachikulu cha kuchezera kwa woyang’anira dera n’chotani, ndipo tiyenera kutani kuti tipindule ndi kuchezera kwake? [od-CN tsa. 48 ndime 3]
9. Kodi timapindula bwanji ndi khama ndi chisamaliro chachikondi cha oyang’anira achikhristu okhwima mwauzimu? [od-CN tsa. 53 ndime 4]
10. Kodi n’chiyani chingathandize wokamba nkhani kuti asachite kulemba notsi zochuluka? [be-CN tsa. 42 ndime 1]
KUWERENGA BAIBULO KWA MLUNGU NDI MLUNGU
11. Kodi ‘omwe amafuna Yehova amamvetsetsa zonse’ m’njira yotani? (Miy. 28:5)
12. Kodi ndi motani mmene ‘ntchito ya zitsiru imazitopetsera zonsezo’? (Mlal. 10:15)
13. Kodi Msulami anasonyeza bwanji kuti anali ngati “munda wotsekedwa,” ndipo ndi motani mmene alili chitsanzo chabwino kwa akazi achikhristu osakwatiwa? (Nyimbo 4:12)
14. Mwa kupempha Aisiraeli kuti ‘akonze zinthu,’ kodi Yehova anali kusonyeza kuti ndi wokonzeka kukambirana nawo kuti agwirizane pa mfundo zomwe zingakhale zabwino kwa iyeyo ndi anthu akewo? (Yes. 1:18a, NW)
15. Kodi lemba la Yesaya 11:6-9 linakwaniritsidwa bwanji mu nthawi zakale, ndipo kodi kukwaniritsidwa kwake kwakukulu n’kotani?