Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/05 tsamba 3
  • Zilengezo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zilengezo
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
km 11/05 tsamba 3

Zilengezo

◼ Mabuku ogawira mu November: Gawirani buku la Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso. Ngati eninyumba akuoneka kuti alibe ana, gawirani buku la Chidziŵitso kapena thirakiti lakuti Kodi Mukufuna Kudziŵa Zambiri za Baibulo? December: Gawirani buku la Munthu Wamkulu Koposa Onse Amene Anakhalako. January: Gawirani bulosha la Dikirani! February: Gawirani buku la Yandikirani kwa Yehova.

◼ Woyang’anira wotsogolera kapena wina amene iye wam’sankha awerengere maakaunti a mpingo pa December 1, kapena patangodutsa masiku ochepa kuchokera pa detili. Akamaliza kuwerengerako, mukalengeze kumpingo powerenga lipoti lotsatira la maakaunti.

◼ Ngati munthu walemba macheke a zopereka okaika m’mabokosi a m’Nyumba ya Ufumu a zopereka za ntchito ya padziko lonse ndi za Thumba la Nyumba za Ufumu, azilemba pamachekepo kuti ndalamazo apatse “Watch Tower Society.” Zopereka za m’macheke za pamsonkhano wa chigawo ndi zonse zotumizidwa ku nthambi zizilembedwanso kuti apatse “Watch Tower Society.” Adiresi ya ofesi yoona za ndalama ya ku nthambi ndi iyi: Watch Tower Bible and Tract Society, Box 30749, Lilongwe 3.

◼ Tikukumbutsa ofalitsa onse a mpingo kuti azipereka lipoti la utumiki wawo wa kumunda mwamsanga pamapeto pa mwezi uliwonse. N’chizolowezi chabwino kuti oyang’anira Phunziro la Buku la Mpingo azitenga masilipi a malipoti (S-4) popita ku phunziro la buku lomaliza la mwezi uliwonse kotero kuti azikumbutsa ofalitsa a m’gulu lawo za kufunika kopereka malipoti ndipo azipereka masilipi osalembapo kanthu kwa amene angawafune. Popereka malipoti a mwezi uliwonse, tiyenera kukumbukira kuti mlembi wa mpingo amafunikira kukhala atatumiza malipotiwa pofika pa sikisi pa mwezi wotsatira. Malipoti amene talandira akusonyeza kuti ofalitsa ambiri sapereka malipoti awo mwamsanga kuti mlembi awatumize panthawi yake. M’mipingo ina mlembi amayembekezera kufikira ofalitsa onse atapereka malipoti awo kuti awatumize. Imeneyi si njira yabwino. Malipoti a utumiki wa kumunda (S-4) onse ochedwa ayenera kusungidwa pambali n’kudzaphatikizidwa ndi malipoti a mwezi wotsatira opita ku ofesi ya nthambi. Alembi onse a mipingo akukumbutsidwa kutumiza lipoti la mpingo (S-1) kudzera ku positi ofesi nthawi yabwino. Mlembi wa mpingo ndi woyang’anira Phunziro la Buku la Mpingo ali ndi udindo woonetsetsa kuti alandira malipoti a kutimagulu tonse ndi kuwatumiza ku ofesi ya nthambi pasanafike pa sikisi pa mwezi wotsatira.

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena