Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w01 9/1 tsamba 13
  • Kale Tinali Mimbulu—Tsopano Ndife Nkhosa!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kale Tinali Mimbulu—Tsopano Ndife Nkhosa!
  • Nsanja ya Olonda—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Kuchokera ku Tondovi Kumka ku Chimwemwe
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • “M’kamwa mwa Makanda”
    Nsanja ya Olonda—1995
Nsanja ya Olonda—2001
w01 9/1 tsamba 13

Kale Tinali Mimbulu​—Tsopano Ndife Nkhosa!

Ine ndi Sakina tinali kukhala moyandikana tili aang’ono. Sakina anali wamkulu thupi ndiponso wamphamvu pamene ine ndinali wamng’ono ndi woonda. Tinali kukangana nthaŵi zambiri, moti tsiku lina tinatidzimulana modetsa nkhaŵa. Kuyambira tsiku limenelo, tinaleka kulankhulana ngakhale kupatsana moni. M’kupita kwa nthaŵi, tonse tinachoka pamalowo ndipo aliyense sankadziŵa kumene mnzake anali kukhala.

Mu 1994, ndinayamba kuphunzira Baibulo ndi Mboni za Yehova, ndipo khalidwe langa linasintha pang’ono ndi pang’ono. Patapita zaka zinayi, ndinali pa msonkhano wapadera watsiku limodzi ku Bunjumbura, Burundi, ndipo ndinadabwa kukumana mwadzidzidzi ndi Sakina. Ndinasangalala kuti anafika pamsonkhanowu, komabe tinalonjerana momangika. Ndinadabwa kwambiri tsiku limenelo kumuona ali pagulu la anthu oti abatizidwe. Iyenso anali atasinthiratu. Sanalinso munthu wamphulupulu amene ndinali kukangana naye nthaŵi zambiri. Zinalitu zosangalatsa kumuona akusonyeza poyera kudzipatulira kwake kwa Mulungu mwa kubatizidwa m’madzi!

Atatuluka m’madzi, ndinathamanga kukam’kumbatira. Ndiyeno ndinam’nong’oneza kuti: “Kodi ukukumbukira mmene tinkamenyerana?” Anayankha kuti: “Inde, ndikukumbukira, koma n’zakale zimenezo. Panopa ndine munthu watsopano.”

Tonsefe ndife okondwa kuti tapeza choonadi cha Baibulo chimene chimagwirizanitsa. Ndiponso tili ndi chimwemwe kuti tasintha miyoyo yathu yonga mimbulu n’kukhala monga nkhosa za Mbusa Wamkulu, Yehova Mulungu. Ndithudi, choonadi cha Baibulo chimasintha miyoyo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena