Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w98 1/1 tsamba 32
  • Yankho Logometsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yankho Logometsa
  • Nsanja ya Olonda—1998
Nsanja ya Olonda—1998
w98 1/1 tsamba 32

Yankho Logometsa

NYUZIPEPALA ya Aroma Katolika ku Britain, yakuti Catholic Herald, posachedwapa inafalitsa kalata yotsatirayi yochokera kwa woŵerenga wina wa ku Wales: “Tsiku lina madzulo, Mboni za Yehova ziŵiri zinafika pakhomo panga. Ndinawauza kuti Tchalitchi cha Katolika nchimene chinalonjeza kuchita mawu enieniwo omwe Mbonizo zinaŵerenga m’Chipangano Chatsopano. Zinandidabwitsa kuti winayo anandivomereza. Anati, ‘Inde, mumalonjeza, koma simumachita. Yesu anati, “mukondane wina ndi mnzake, monga ndakonda inu,” koma inu mumaphana. Pankhondo yapita, Akatolika anapha Akatolika, koma Mboni za Yehova sizinaphe Mboni [inzawo] iliyonse.’ Kodi pamenepo ndikanaleka kuvomereza? Kodi tingapempherere bwanji ‘kugwirizana ndi abale athu apambali’ pomwe tokhatokha sitikugwirizana? Kodi pamenepa sipofunika kuti tithetse kaye nkhani yochititsa manyaziyi?”​—Yohane 15:12.

Nkhondo zadziko zonse ziŵiri za m’zaka za zana la 20 zino zinayambira m’Dziko Lachikristu ndipo zinapha anthu pakati pa mamiliyoni 50 ndi mamiliyoni 60. Komabe, tinganene motsimikiza kuti Mboni za Yehova sizinatenge nawo mbali pankhondo zimenezo, ndipo sizimaloŵerera m’mikangano iliyonse imene ikuchitika lerolino. Kodi zimenezo zimatheka bwanji? Mungapindule kwambiri mutadziŵa za kugwirizana kolimba kwa chikondi ndi umodzi wachikristu kumene kukupezeka pakati pa Mboni za Yehova zoposa mamiliyoni asanu padziko lonse.​—Yerekezerani ndi Yesaya 2:4.

[Mawu a Chithunzi patsamba 32]

Chithunzi cha U.S. National Archives

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena