Iwo Amachita Zimene Angathe
Ngakhale kuti sali okhoza kumbwezera Yehova kaamba ka zabwino zake zonse kwa iwo, ambiri amachita zimene angathe kuchirikiza ntchito yolalikira yapadziko lonse ya Mboni zake. (Mateyu 24:14; yerekezerani ndi Marko 14:3-9.) Kalata iyi yochokera ku banja la ku Minnesota, U.S.A. iri yosangalatsa:
“Abale Okondedwa,
“Tikutumiza chopereka cha unyinji wa $——. Tikupempha kuti chigwiritsiridwe ntchito kulipirira ntchito yapadziko lonse kapena kuperekedwa ku Thumba la Ndalama za Nyumba Yaufumu, kapena ku chosoŵa china chirichonse chimene gulu lingakhale nacho. . . .
“Ndife achidaliro kuti ndalamazi zidzagwiritsiridwa ntchito mogwirizana ndi chifuniro cha [Yehova]. Tingakonde kugwiritsira ntchito mwaŵiwu kukulimbikitsani kupitiriza ntchito yabwinoyi, ndipo makamaka tikuthokozani chifukwa cha “videotape” ya kagwiridwe ka ntchito ka padziko lonse ka [Watch Tower] Society. Inali tepi imeneyi imene inatizindikiritsa za ntchito yaikuluyo, ndipo inakhomereza m’maganizo mwathu kuti zopereka zathu zodzifunira zimafunidwa. Kalelo, tinalekera mpingo, dera, ndi chigawo kusamalira zokutumizirani zopereka, koma tsopano tikuthokoza Yehova chifukwa chokhala woleza mtima ndi kusawona patali kwathu ndikutisonyeza mwachikondi kufunika kwa kuthandiza mwaumwini kulipirira ntchito yopulumutsa moyoyi, kuwonjezera pa zopereka zina. Monga banja, tamvana kumatumiza mwachindunji ku New York unyinji wosachepera wa $——pamwezi.
“Kachiŵirinso, tikuthokozani kaamba ka utumiki wabwino umene mumatichitira ndi kukhulupirika kwanu kwa Yehova kumene mwakusonyeza.”