Kodi Sayansi Ingatsutse Zozizwitsa?
Kodi zozizwitsa za m’Baibulo zinachitikadi? Pali ambiri, kuphatikizapo asayansi ndi atsogoleri achipembedzo, amene amayankha kuti ayi. Iwo amaganiza kuti kukhulupirira zozizwitsa kuli kwa m’nyengo yamalaulo ndikuti sayansi yamakono yatsutsa kuthekera kwa kuchitika kwake. Chifukwa chake, kalata yotsatirayi yofalitsidwa mu The Times ya ku London ndi kusainidwa ndi asayansi ambiri iyenera kulingaliridwa. Iyo imati:
“Sikuli kokhutiritsa mwanzeru kugwiritsira ntchito sayansi monga yotsutsira zozizwitsa. Kukhulupirira kuti zozizwitsa sizingachitike kuli kwakukulukulu nkhani ya chikhulupiriro mofanana ndi kukhulupirira kuti zingachitike. . . . Zozizwitsa ziri zinthu zomwe sizinachitikepo. Mosasamala kanthu za malingaliro amene angaperekedwe ndi nthanthi kapena zivumbulutso zamakono, kuli kofunika kutsimikizira kuti sayansi (monga momwe iriri yozikidwa pa kufotokoza zinthu zomwe zinachitikapo) singanene chirichonse pankhaniyi. ‘Malamulo’ ake ali kokha kulankhula mwachisawawa zokumana nazo zathu. Chikhulupiriro chimayedzamira pa maziko ena.” (Kanyenye ngwathu.) Ndithudi, palibe njira iriyonse imene sayansi yamakono ingatsutsire nkhani za zozizwitsa zolembedwa m’Baibulo.