“Kuyankha Mowongoka”
MU ULALIKI wa pa Phiri, Yesu analozera ku “chilamulo ndi aneneri.” Mbali yachitatu ya Malemba Achihebri inali Zolembedwa, zimene zinaphatikizapo mabukhu a ndakatulo, onga ngati Masalmo ndi Miyambo. (Mateyu 7:12; Luka 24:44) Awanso, anali ndi nzeru ya Mulungu.
Mwachitsanzo, miyamboyo inachenjeza oweruza mu Israyeli wakale kuti: “Wonena kwa woipa, wolungama iwe; magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira. Omwe amdzudzula adzasekera, nadzadalitsika ndithu. [Woyankha mowongoka, NW] apsompsona milomo.”—Miyambo 24:24-26.
Ngati woweruza anagonjera ku zididikizo za chiphuphu kapena wako ndi wako ndi kulengeza woipa kukhala wolungama, ena akamuwona iye kukhala wosayenera malo ake. Nkulekeranji, popeza kuti ngakhaledi ziŵalo za Amitundu “magulu a mitundu” omwe anamva za kupotozedwa kwa chiweruzo koteroko ankaipidwa! Ku mbali ina, ngati woweruza molimba mtima anadzudzula munthu woipa ndi kumyankha mowongoka pa mlandu wozengedwawo, iye akapeza ulemu ndi kukondedwa ndi anthuwo. Anthu onsewo akafulumizidwa kumfunira iye “madalitso abwino.” Monga momwe mwambiwo ukuchiikira mowonjezereka kuti: “[Woyankha mowongoka, NW] apsompsona milomo.”
Kupsompsona koteroko kunatanthauza kulemekezana—pakati pa phungu ndi awo olabadira chidzudzulo chake chowongoka. Mwinamwake ngakhale yemwe akudzudzulidwa akachitapo kanthu moyanja ndi kusonyeza kukonda kwake woweruzayo. Miyambo 28:23 ikutero kuti: “Adzamkomera mtima wodzudzula mtsogolo mwake, koposa wosyasyalika ndi lilime lake.” Chotero awo otumikira monga akulu a mpingo lerolino ayenera kupeŵa kulola ubwenzi kapena unansi wa banja kuipitsa chiweruzo chawo. Mwa kupereka uphungu wofunikira mowongoka, akulu adzapeza ulemu mu mpingo.