Revelation—Its Grand Climax At Hand!
Umenewo ndiwo mutu wa bukhu latsopano limene limakambitsirana mwatsatanetsatane bukhu lonse la Baibulo la Chibvumbulutso. Muŵerengi wachisangalalo wa ku California akulemba kuti:
“Ndimalikonda ilo! Ndimakonda mwapadera kapangidwe kake. Malemba okhala m’zirembo zazikulu, zakuda, ndi malongosoledwe omvekera bwino, olunjika, ndi omvetsetseka operekedwa a lemba lirilonse. Limapanga kaamba ka kuŵerenga kopepuka. ndimayamikiranso kufupika kwa mituyo. Matchati ndi zisonyezero zomathandiza mowonjezereka.
“Tangoganizirani, monga mkazi wa panyumba ndingakhale pansi kuŵerenga ndi kumvetsetsa zinthu zakuya za Mulungu. Chifukwa munatenga nthaŵi ndi chisamaliro kupepukitsa nkhani zimenezi, ife tonse tingakule kuyandikira chifupi kwa Mulungu wathu.”
Inu mudzasangalatsidwa ndi kuzindikiritsidwa komvekera bwino, ndi kwanzeru kwa zirombo, chinjoka, mkazi wachigololo wamkulu, ndi zinthu zina za chizindikiro za Chibvumbulutso. Mudzawona tanthauzo kaamba ka tsiku lathu. Bukhu la chikuto cholimba lochititsa chidwi limeneli, la ukulu wa masamba ofanana ndi magazini ino, limapereka kulingaliridwa kwa Chibvumbulutso kwa ndime ndi ndime. Tumizani kaamba ka ilo lero. Kokha K30, titalipiriratu positi.
Chonde tumizani bukhu la masamba 320 Revelation--Its Grand Climax At Hand! Ndatsekeramo K30 (Zambia).