‘Sindinayembekezere Kusangalala Nalo’
CHIMENECHO ndi chimene munthu analembera bwenzi lomwe linatumiza kope la mphatso la bukhu la Life—How Did It Get Here? By Evolution or by Creation? “Ndiri wotsimikizira kuti unadabwa ngati ndinalandira bukhulu,” munthuyo analemba tero. “Inde! Zikomo! Kodi ndinaliŵerenga ilo? Kachiŵirinso inde. Ndinali wodabwitsidwa kwambiri kulipeza ilo kukhala losangalatsa.
“Sindinayembekezere nkomwe kusangalala nalo, m’chenicheni, ndinangoliyamba ilo kotero kuti ndinganene kwa inu kuti ‘Chabwino, ndinayesera.’ Ku kukhumudwitsidwa kwanga sindinakhoze kuliika ilo pambali. . . . Chinatenga mwinamwake masiku 10 kulimaliza. Ndinadabwitsidwa. Mwamsanga ndinauza mabwenzi ena ponena za ilo—kulibwereketsa ilo kwa aŵiri a iwo ndi kulilonjeza kwa wachitatu! Chotero chifupifupi 4 a ife pano tidzaliŵerenga ilo ndi ena owonjezereka, ndikuyembekezera tero. Ilo liridi bukhu losangalatsa kwambiri. Kachiŵirinso, zikomo.”
Kodi mukudziŵa winawake kwa amene mungatumize bukhu limene iye angalikonde mowonadi? Chotero bwanji osatumiza kope ya mphatso ya Life—How Did It Get Here? By Evolution or by Creation? Mungachite tero mwa kungodzaza ndi kutumiza kapepala kali pansipa, kutsekeramo kokha K24 ndi kapepalako.
Chonde tumizani, mutalipiriratu positi, kope ya mphatso ya bukhu la masamba 256 Life—How Did It Get Here? By Evolution or by Creation? limodzinso ndi kalata yolongosola kuti iri mphatso yochokera kwa (dzina lanu). Ndatsekeramo K24 (Zambia).