Iwo Anadabwitsidwa Kuwona Ine Ndikuŵerenga Iwo
Wachichepere wochokea ku Philippines akulemba kuti: “Ndiri wophunzira wa pa sukulu yampamwamba wa chaka choyamba ndi m’Katolika wodzipereka. Pamene bwenzi langa linandiwunikira ine ku Galamukani! ndi Nsanja ya Olonda, ndinalandira iwo. Ndinapeza iwo kukhala osangalatsa kwambiri ngakhale kuti amafalitsidwa ndi Mboni za Yehova. Pamene ndinali kuŵerenga iwo m’kalasi mwathu, anzanga a m’kalasi anadabwitsidwa, popeza ndinali m’Katolika. Ndinapatsa anzanga a m’kalasimo imodzi, ndipo nawonso anaikonda. Magaziniyo inafikiranso mphunzitsi wanga wachipembedzo, ndipo mphunzitsi ameneyu anasonyeza chikondwerero, popeza inachita ndi mavuto a makhalidwe abwino a lerolino. Ndikuyembekeza kuti mudzapitiriza kusindikiza kumeneku.”
Inunso mungapeze magaziniwa kukhala othandiza kwambiri m’kuphunzira maprinsipulo a Baibulo. Mungakhale ndi iwo akutumizidwa kunyumba kwanu mwa kudzaza ndi kutumiza kapepala kotsatiraka. Kokha K48.
Chonde tumizani kulembetsa kwa chaka chimodzi kwa Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Ndatsekeramo K48 (Zambia). (Kunja kwa Zambia, lemberani nthambi ya Watch Tower ya kwanuko kaamba ka chidziŵitso.)