Anayamikiridwa ndi Dokotala wa Zamankhwala
Dokotala wa zamankhwala mu Frankfurt, West Germany, yemwe anaitanidwa kulembetsanso kulembetsa kwake kwa magazini a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani!, sanatumize kokha ndalama kaamba ka kulembetsansoko koma analongosola kuti:
“Ndimazizwitsidwa nthaŵi zonse kupeza kuperekedwa kokulira chotere kwa nkhani zabwino kwambiri ndi zokondweretsa—zambiri za izo zomwe ziri zosakhoza ngakhale kulongosoledwa ndi chipembedzo—pamtengo wotsika chotere. Ngakhale kuti ndiri ndi nthaŵi yochepera kaamba ka inemwini, madzulo anga onse ankatsirizidwa kaŵirikaŵiri wotsekeredwa m’chipinda changa ndikuŵerenga magazini anu nditayatsa nyali. Kachiŵirinso, ndikupereka kuyamikira kotentha kaamba ka kuyesayesa kwanu.
Bwanji osasangalala ndi kuŵerenga magazini yabwino kwambiri imeneyi inueni? Inu mungakhale ndi magazini odzetsa phindu aŵiriwa akuperekedwa kunyumba kwanu mwa kudzaza ndi kutumiza kapepala kotsatiraka.
Chonde tumizani kulembetsa kwa chaka chimodzi kaamba ka Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Ndatsekeramo K48.00 (Zambia). (Kunja kwa Zambia, lemberani ku nthambi ya Watch Tower ya kwanuko kaamba ka chidziŵitso.)