Kupirira Pansi pa Chitsenderezo cha Mphamvu Yoposa Munthu
Kodi mumadzimva kuti ichi ndi chimene mukuchita?
Anthu ambiri amatero. Ndipo iwo athandizidwa m’kudziŵa mmene ena akuchitira. Kalata yochokera ku Greenville, Texas, yolemberedwa ku Watchtower Society, inalongosola kuti: “Mowonadi ndimayamikira nkhani zenizeni za moyo za Akristu omwe apirira kuvutika kwambiri ndi cholinga chofuna kukhala okhulupirika. Zambiri zinali zokumana nazo zimene ndinaŵerenga ndi misozi ikutsika m’maso mwanga, monga mmene ndinawonera kuti kokha Yehova Mulungu wowona anali wokhoza kuwapulumutsa iwo kuchokera ku matsoka oterowo amene iwo analimo. Chimandipangitsa ine kukhala Mkristu wodzichepetsa ndi woyamikira pamene ndiŵerenga zimene iwo anapyolamo, ndipo linandithandiza ine kusalingalira mokulira ponena za inemwini kapena kukhala wadyera.”
1988 Yearbook of Jehovah’s Witnesses yadzazidwa ndi zokumana nazo za kaimidwe kolimba ka Akristu kaamba ka chilungamo mkati mwa nkhondo mu Korea ndi mkati mwa zaka za uchigawenga mu Ireland. Yearbook yaperekanso nkhani ya mbiri yakale ya Mboni za Yehova mu Costa Rica, ndiponso ndi chithunzi chamakono cha ntchito yawo pa dziko lonse.
Chonde tumizani, mutalipiriratu positi, 1988 Yearbook of Jehovah’s Witnesses. Ndatsekeramo K8.00.