‘Kuti Lichotse Kusungulumwa Kwake’
MWAMUNA WINA amene anapita kukagwira ntchito ku Sultanate ya Oman analembera ofesi ya nthambi ya Watch Tower Society mu India. “Masiku pang’ono apitawa,“ iye anati, “ndinawona bukhu la Happiness—How to Find It mu nyumba ya m’modzi wa anzanga konkuno. Nchosafuna kuchita kunena kuti bukhu lonselo liridi chinthu chamtengo wapatali. Kunena zowona, bukhu laling’ono limeneli landithandiza ine kwambiri, ndipo ndikufuna kupereka bukhu lomweli monga mphatso yatsiku lokumbukira ukwati wathu kwa mkazi wanga monga mphatso ya kuchotsa kusungulumwa kwake. Mwachikondi ndichitireni chifundo mwa kunditumizira kope la bukhu limeneli kwa mkazi wanga m’malo mwa ine mwamsanga monga mmene kumwambapa.”
Bukhu limeneli la masamba 192 sirimapereka kokha thandizo lolimbikitsa mukuchita ndi mikhalidwe yotsendereza koma limaloza ku njira ya mayankho osatha ku mavuto amoyo.
Chonde nditumizireni, mutalipiriratu positi, bukhu la chikuto cholimba la Happiness—How to Find It (m’Chingelezi). Ndatumiza K5. 00.