Kusakaza Kokulira kwa Fodya mu Greece
AKUMAKULITSA pa mutu womveka wa nyimbo ya Chigriki, wochitira ripoti analemba ndi mawu ogwira mtima kuti: “Inde, ‘Grisi Sakufa,’ koma Agriki amafa.”
“Anthu zikwi khumi amafa chaka chirichonse chifukwa cha kusuta, m’dziko lathu lokha,” inachitira ripoti tero nkhani mu nyuzipepala ya Chiathenian Eleftheros Typos. Ena amakhulupirira kuti kusakaza kowona kokulira kwa fodya kungakhale kokulira kuwirikiza kaŵiri. Greece liri dziko lolima fodya, ndipo kusuta kuli chizoloŵezi chomakulakulabe pakati pa Agriki mosasamala kanthu za maripoti ambiri omwe alembedwa posachedwapa onena za ngozi yochititsidwa ndi kusuta.